< Masalimo 145 >
1 Salimo la matamando la Davide. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga; ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
(En Lovsang af David.) Jeg vil ophøje dig, min Gud, min konge, evigt og alt love dit Navn.
2 Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
Jeg vil love dig Dag efter Dag, evigt og altid prise dit Navn.
3 Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse; ukulu wake palibe angawumvetsetse.
Stor og højlovet er HERREN, hans Storhed kan ikke ransages.
4 Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina; Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
Slægt efter Slægt lovpriser dine Værker, forkynder dine vældige Gerninger.
5 Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu, ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
De taler om din Højheds herlige Glans, jeg vil synge om dine Undere;
6 Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri, ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
de taler om dine ræddelige Gerningers Vælde, om din Storhed vil jeg vidne;
7 Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu, ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
de udbreder din rige Miskundheds Ry og synger med Fryd om din Retfærd.
8 Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
Nådig og barmhjertig er HERREN, langmodig og rig på Miskundhed.
9 Yehova ndi wabwino kwa onse; amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
God er HERREN mod alle, hans Barmhjertighed er over alle hans Værker.
10 Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova; oyera mtima adzakulemekezani.
Dine Værker takker dig alle, HERRE, og dine fromme lover dig.
11 Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
De forkynder dit Riges Ære og taler om din Vælde
12 kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
for at kundgøre Menneskenes Børn din Vælde, dit Riges strålende Herlighed.
13 Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse. Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
Dit Rige står i al Evighed, dit Herredømme varer fra Slægt til Slægt. (Trofast er HERREN i alle sine Ord og miskundelig i alle sine Gerninger).
14 Yehova amagwiriziza onse amene akugwa ndipo amakweza onse otsitsidwa.
HERREN støtter alle, der falder, og rejser alle bøjede.
15 Maso a onse amayangʼana kwa Inu, ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
Alles Øjne bier på dig, du giver dem Føden i rette Tid;
16 Mumatsekula dzanja lanu ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
du åbner din Hånd og mætter alt, hvad der lever, med hvad det ønsker.
17 Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse, ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
Retfærdig er HERREN på alle sine Veje, miskundelig i alle sine Gerninger.
18 Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana, onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
Nær er HERREN hos alle, som kalder, hos alle, som kalder på ham i Sandhed.
19 Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa; amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
Han gør, hvad de, der frygter ham, ønsker, hører deres Råb og frelser dem,
20 Yehova amayangʼana onse amene amamukonda koma adzawononga anthu onse oyipa.
HERREN vogter alle, der elsker ham, men alle de gudløse sletter han ud.
21 Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova. Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera ku nthawi za nthawi.
Min Mund skal udsige HERRENs Pris, alt Kød skal love hans hellige Navn evigt og altid.