< Masalimo 145 >
1 Salimo la matamando la Davide. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga; ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
Jeg vil ophøje dig, min Gud, du som er Kongen! og love dit Navn evindelig og altid.
2 Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
Hver Dag vil jeg love dig og prise dit Navn evindelig og altid.
3 Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse; ukulu wake palibe angawumvetsetse.
Herren er stor og saare priselig, og hans Magt er uransagelig.
4 Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina; Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
En Slægt skal berømme for den anden dine Gerninger, og de skulle forkynde din Vælde.
5 Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu, ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
Jeg vil betænke din Majestæts herlige Ære og dine underfalde Gerninger.
6 Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri, ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
Og der skal tales om dine forfærdelige Gerningers Vælde, og jeg vil fortælle om din Magt.
7 Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu, ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
De skulle udbrede din store Godheds Ihukommelse og synge med Fryd om din Retfærdighed.
8 Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
Herren er naadig og barmhjertig, langmodig og af stor Miskundhed.
9 Yehova ndi wabwino kwa onse; amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
Herren er god imod alle, og hans Barmhjertighed er over alle hans Gerninger.
10 Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova; oyera mtima adzakulemekezani.
Dig, Herre! skulle alle dine Gerninger prise og dine hellige love dig.
11 Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
De skulle forkynde dit Riges Ære, tale om din Vælde,
12 kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
for at kundgøre for Menneskens Børn hans Vælde og hans Riges herlige Ære.
13 Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse. Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
Dit Rige er et Rige i al Evighed, og dit Herredømme varer fra Slægt til Slægt.
14 Yehova amagwiriziza onse amene akugwa ndipo amakweza onse otsitsidwa.
Herren opholder alle dem, som falde, og oprejser alle de nedbøjede.
15 Maso a onse amayangʼana kwa Inu, ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
Alles Øjne vogte paa dig, og du giver dem deres Spise i sin Tid.
16 Mumatsekula dzanja lanu ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
Du oplader din Haand og mætter alt det, som lever, med Velbehagelighed.
17 Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse, ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
Herren er retfærdig i alle sine Veje og miskundelig i alle sine Gerninger.
18 Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana, onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
Herren er nær hos alle, som kalde paa ham, hos alle, som kalde paa ham i Sandhed.
19 Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa; amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
Han gør efter deres Velbehagelighed, som ham frygte, og han hører deres Skrig og frelser dem.
20 Yehova amayangʼana onse amene amamukonda koma adzawononga anthu onse oyipa.
Herren bevarer alle dem, som elske ham, men han ødelægger alle de ugudelige.
21 Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova. Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera ku nthawi za nthawi.
Min Mund skal udtale Herrens Lov, og alt Kød skal love hans hellige Navn evindelig og altid.