< Masalimo 144 >

1 Salimo la Davide. Atamandike Yehova Thanthwe langa, amene amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; zala zanga kumenya nkhondo.
Dawid de. Nkamfo nka Awurade, me Botan, nea ɔma me nsa akodi ho ntetewee, ne me nsateaa ma ɔsa.
2 Iye ndiye Mulungu wanga wachikondi ndi malo anga otetezedwa, linga langa ndi mpulumutsi wanga, chishango changa mmene ine ndimathawiramo, amene amagonjetsa mitundu ya anthu pansi panga.
Ɔyɛ mʼadɔe Nyankopɔn ne mʼabandennen, me bammɔ ne me gyefo, me kyɛm a mewɔ guankɔbea wɔ no mu, ɔno na ɔka nnipa hyɛ mʼase.
3 Inu Yehova, munthu nʼchiyani kuti mumamusamalira, mwana wa munthu kuti muzimuganizira?
Awurade, hena ne onipa a wʼani ku no ho onipa ba a wudwen ne ho yi?
4 Munthu ali ngati mpweya; masiku ake ali ngati mthunzi wosakhalitsa.
Onipa te sɛ ɔhome; ne nna te sɛ sunsuma a ɛretwa mu.
5 Ngʼambani mayiko akumwamba, Inu Yehova, ndipo tsikani pansi; khudzani mapiri kuti atulutse utsi.
Awurade, fi ɔsoro hɔ na sian bra fam; fa wo nsa ka mmepɔw, na emfi wusiw.
6 Tumizani zingʼaningʼani ndi kubalalitsa adani; ponyani mivi yanu ndi kuwathamangitsa.
Soma anyinam na bɔ atamfo no hwete; to wo mmɛmma no ma wonguan.
7 Tambasulani dzanja lanu kuchokera kumwamba; landitseni ndi kundipulumutsa, ku madzi amphamvu, mʼmanja mwa anthu achilendo,
Teɛ wo nsa fi ɔsoro bra fam; gye me na yi me fi nsu akɛse ho, fi ananafo nsam,
8 amene pakamwa pawo ndi podzala ndi mabodza, amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.
wɔn a atoro ayɛ wɔn anom ma, na wɔn nsa nifa yɛ nnaadaa.
9 Ndidzakuyimbirani nyimbo yatsopano Inu Mulungu; ndidzakuyimbirani nyimbo pa zeze wa nsambo khumi,
Onyankopɔn, mɛto dwom foforo ama wo; mɛto dwom wɔ sanku a ahama du gu so so ama wo,
10 kwa Iye amene amapambanitsa mafumu, amene amapulumutsa Davide mtumiki wake ku lupanga loopsa.
ama Ɔbaako a ɔde nkonimdi ma ahemfo, na ogye ne somfo Dawid fi afoawerɛmfo ano.
11 Landitseni ndi kundipulumutsa, mʼmanja mwa anthu achilendo, amene pakamwa pawo ndi podzaza ndi mabodza, amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.
Gye me na yi me fi ananafo nsam, wɔn a atoro ayɛ wɔn anom ma na wɔn nsa nifa yɛ nnaadaa.
12 Ndipo ana aamuna pa chinyamata chawo adzakhala ngati mbewu yosamalidwa bwino, ana athu aakazi adzakhala ngati zipilala zosemedwa bwino, zokongoletsera nyumba yaufumu.
Afei yɛn mmabarima mmerantebere mu bɛyɛ sɛ afifide a wɔahwɛ so yiye, na yɛn mmabea bɛyɛ sɛ adum a wɔasen de asiesie ahemfi.
13 Nkhokwe zathu zidzakhala zodzaza ndi zokolola za mtundu uliwonse. Nkhosa zathu zidzaswana miyandamiyanda pa mabusa athu.
Yɛn asan bɛyɛ amaama; aduan ahorow biara bɛba so. Yɛn nguan dodow so bɛto mpem mpem, wɔn so bɛto mpem du du wɔ yɛn mfuw so;
14 Ngʼombe zathu zidzanyamula katundu wolemera. Sipadzakhala mingʼalu pa makoma, sipadzakhalanso kupita ku ukapolo, mʼmisewu mwathu simudzakhala kulira chifukwa cha mavuto.
yɛn anantwi bɛtwe nnesoa duruduru. Wɔrennwiriw afasu, yɛrenkɔ nkoasom mu, na agyaadwotwa remma yɛn mmɔnten so.
15 Odala anthu amene adzalandira madalitso awa; odala anthu amene Mulungu wawo ndi Yehova.
Nhyira nka nnipa a ɛbɛba mu saa ama wɔn. Nhyira nka nnipa a wɔn Nyankopɔn ne Awurade.

< Masalimo 144 >