< Masalimo 144 >

1 Salimo la Davide. Atamandike Yehova Thanthwe langa, amene amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; zala zanga kumenya nkhondo.
Kayibongwe iNkosi, idwala lami, efundisela izandla zami impi, iminwe yami ukulwa;
2 Iye ndiye Mulungu wanga wachikondi ndi malo anga otetezedwa, linga langa ndi mpulumutsi wanga, chishango changa mmene ine ndimathawiramo, amene amagonjetsa mitundu ya anthu pansi panga.
umusa wami, lenqaba yami, umphotshongo wami ophakemeyo, lomkhululi wami, isihlangu sami, lengiphephela kuyo, ethobisa abantu bami ngaphansi kwami.
3 Inu Yehova, munthu nʼchiyani kuti mumamusamalira, mwana wa munthu kuti muzimuganizira?
Nkosi, umuntu uyini ukuthi umazi? Indodana yomuntu ukuthi uyinanze?
4 Munthu ali ngati mpweya; masiku ake ali ngati mthunzi wosakhalitsa.
Umuntu unjengeze, insuku zakhe zinjengesithunzi esidlulayo.
5 Ngʼambani mayiko akumwamba, Inu Yehova, ndipo tsikani pansi; khudzani mapiri kuti atulutse utsi.
Nkosi, khothamisa amazulu akho, wehle; thinta izintaba ukuze zithunqe.
6 Tumizani zingʼaningʼani ndi kubalalitsa adani; ponyani mivi yanu ndi kuwathamangitsa.
Phazimisa umbane, ubachithe, uthumele imitshoko yakho, ubahlakaze.
7 Tambasulani dzanja lanu kuchokera kumwamba; landitseni ndi kundipulumutsa, ku madzi amphamvu, mʼmanja mwa anthu achilendo,
Yelula isandla sakho uphezulu, ungikhulule, ungophule emanzini amanengi, esandleni sabantwana besizwe,
8 amene pakamwa pawo ndi podzala ndi mabodza, amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.
abamlomo wabo ukhuluma amanga, lesandla sabo sokunene singesokunene senkohliso.
9 Ndidzakuyimbirani nyimbo yatsopano Inu Mulungu; ndidzakuyimbirani nyimbo pa zeze wa nsambo khumi,
Ngizahlabelela kuwe ingoma entsha, Nkulunkulu; ngizahlabelela indumiso kuwe ngogubhu olulentambo ezilitshumi.
10 kwa Iye amene amapambanitsa mafumu, amene amapulumutsa Davide mtumiki wake ku lupanga loopsa.
Wena onika amakhosi usindiso, okhulula uDavida inceku yakho enkembeni embi.
11 Landitseni ndi kundipulumutsa, mʼmanja mwa anthu achilendo, amene pakamwa pawo ndi podzaza ndi mabodza, amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.
Ngophula, ungikhulule esandleni sabantwana besizwe, abamlomo wabo ukhuluma amanga, lesandla sabo sokunene singesokunene senkohliso.
12 Ndipo ana aamuna pa chinyamata chawo adzakhala ngati mbewu yosamalidwa bwino, ana athu aakazi adzakhala ngati zipilala zosemedwa bwino, zokongoletsera nyumba yaufumu.
Ukuthi amadodana ethu abe njengezilimo ezikhula ebutsheni bazo, amadodakazi ethu njengamatshe engonsi abazwe njengomfanekiso wesigodlo!
13 Nkhokwe zathu zidzakhala zodzaza ndi zokolola za mtundu uliwonse. Nkhosa zathu zidzaswana miyandamiyanda pa mabusa athu.
Ukuthi iziphala zethu zigcwale ziveze uhlobo ngohlobo; izimvu zethu zizale izinkulungwane, yebo, izinkulungwane ezilitshumi emadlelweni ethu!
14 Ngʼombe zathu zidzanyamula katundu wolemera. Sipadzakhala mingʼalu pa makoma, sipadzakhalanso kupita ku ukapolo, mʼmisewu mwathu simudzakhala kulira chifukwa cha mavuto.
Ukuthi inkabi zethu zingathwaliswa, kungabi lokufohlela phakathi, njalo kungabi lokuphuma, kumbe kungabi lesililo ezitaladeni zethu!
15 Odala anthu amene adzalandira madalitso awa; odala anthu amene Mulungu wawo ndi Yehova.
Bayathaba abantu okunjalo kubo; bayathaba abantu abaNkulunkulu wabo yiNkosi.

< Masalimo 144 >