< Masalimo 144 >

1 Salimo la Davide. Atamandike Yehova Thanthwe langa, amene amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; zala zanga kumenya nkhondo.
De David. Béni soit Yahweh, mon rocher, qui a dressé mes mains au combat, et mes doigts à la guerre,
2 Iye ndiye Mulungu wanga wachikondi ndi malo anga otetezedwa, linga langa ndi mpulumutsi wanga, chishango changa mmene ine ndimathawiramo, amene amagonjetsa mitundu ya anthu pansi panga.
mon bienfaiteur et ma forteresse, ma haute retraite et mon libérateur, mon bouclier, celui qui est mon refuge, qui range mon peuple sous moi!
3 Inu Yehova, munthu nʼchiyani kuti mumamusamalira, mwana wa munthu kuti muzimuganizira?
Yahweh, qu’est-ce que l’homme pour que tu le connaisses, le fils de l’homme, pour que tu prennes garde à lui?
4 Munthu ali ngati mpweya; masiku ake ali ngati mthunzi wosakhalitsa.
L’homme est semblable à un souffle, ses jours sont comme l’ombre qui passe.
5 Ngʼambani mayiko akumwamba, Inu Yehova, ndipo tsikani pansi; khudzani mapiri kuti atulutse utsi.
Yahweh, abaisse tes cieux et descends; touche les montagnes, et qu’elles s’embrasent;
6 Tumizani zingʼaningʼani ndi kubalalitsa adani; ponyani mivi yanu ndi kuwathamangitsa.
fais briller les éclairs, et disperse les ennemis; lance tes flèches, et mets-les en déroute.
7 Tambasulani dzanja lanu kuchokera kumwamba; landitseni ndi kundipulumutsa, ku madzi amphamvu, mʼmanja mwa anthu achilendo,
Etends tes mains d’en haut, délivre-moi et sauve-moi des grandes eaux, de la main des fils de l’étranger,
8 amene pakamwa pawo ndi podzala ndi mabodza, amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.
dont la bouche profère le mensonge, et dont la droite est une droite parjure.
9 Ndidzakuyimbirani nyimbo yatsopano Inu Mulungu; ndidzakuyimbirani nyimbo pa zeze wa nsambo khumi,
Ô Dieu, je te chanterai un cantique nouveau, je te célébrerai sur le luth à dix cordes.
10 kwa Iye amene amapambanitsa mafumu, amene amapulumutsa Davide mtumiki wake ku lupanga loopsa.
Toi qui donnes aux rois la victoire, qui sauves du glaive meurtrier David, ton serviteur,
11 Landitseni ndi kundipulumutsa, mʼmanja mwa anthu achilendo, amene pakamwa pawo ndi podzaza ndi mabodza, amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.
délivre-moi et sauve-moi de la main des fils de l’étranger, dont la bouche profère le mensonge, et dont la droite est une droite parjure.
12 Ndipo ana aamuna pa chinyamata chawo adzakhala ngati mbewu yosamalidwa bwino, ana athu aakazi adzakhala ngati zipilala zosemedwa bwino, zokongoletsera nyumba yaufumu.
Que nos fils, comme des plants vigoureux, grandissent en leur jeunesse! Que nos filles soient comme les colonnes angulaires, sculptées à la façon de celles d’un temple!
13 Nkhokwe zathu zidzakhala zodzaza ndi zokolola za mtundu uliwonse. Nkhosa zathu zidzaswana miyandamiyanda pa mabusa athu.
Que nos greniers soient remplis, et regorgent de toutes sortes de provisions! Que nos brebis, dans nos pâturages, se multiplient par milliers et par myriades!
14 Ngʼombe zathu zidzanyamula katundu wolemera. Sipadzakhala mingʼalu pa makoma, sipadzakhalanso kupita ku ukapolo, mʼmisewu mwathu simudzakhala kulira chifukwa cha mavuto.
Que nos génisses soient fécondes! Qu’il n’y ait dans nos murs ni brèche, ni reddition! Ni cri d’alarme dans nos places publiques!
15 Odala anthu amene adzalandira madalitso awa; odala anthu amene Mulungu wawo ndi Yehova.
Heureux le peuple qui jouit de ces biens! Heureux le peuple dont Yahweh est le Dieu!

< Masalimo 144 >