< Masalimo 144 >

1 Salimo la Davide. Atamandike Yehova Thanthwe langa, amene amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; zala zanga kumenya nkhondo.
A Psalm of David versus Goliath. Blessed is the Lord, my God, who trains my hands for the battle and my fingers for the war.
2 Iye ndiye Mulungu wanga wachikondi ndi malo anga otetezedwa, linga langa ndi mpulumutsi wanga, chishango changa mmene ine ndimathawiramo, amene amagonjetsa mitundu ya anthu pansi panga.
My mercy and my refuge, my supporter and my deliverer, my protector and him in whom I have hoped: he subdues my people under me.
3 Inu Yehova, munthu nʼchiyani kuti mumamusamalira, mwana wa munthu kuti muzimuganizira?
O Lord, what is man that you have become known to him? Or the son of man that you consider him?
4 Munthu ali ngati mpweya; masiku ake ali ngati mthunzi wosakhalitsa.
Man has been made similar to vanity. His days pass by like a shadow.
5 Ngʼambani mayiko akumwamba, Inu Yehova, ndipo tsikani pansi; khudzani mapiri kuti atulutse utsi.
O Lord, incline your heavens and descend. Touch the mountains, and they will smoke.
6 Tumizani zingʼaningʼani ndi kubalalitsa adani; ponyani mivi yanu ndi kuwathamangitsa.
Send a flash of lightning, and you will scatter them. Shoot your arrows, and you will set them in disarray.
7 Tambasulani dzanja lanu kuchokera kumwamba; landitseni ndi kundipulumutsa, ku madzi amphamvu, mʼmanja mwa anthu achilendo,
Send forth your hand from on high: rescue me, and free me from many waters, from the hand of the sons of foreigners.
8 amene pakamwa pawo ndi podzala ndi mabodza, amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.
Their mouth has been speaking vain things, and their right hand is the right hand of iniquity.
9 Ndidzakuyimbirani nyimbo yatsopano Inu Mulungu; ndidzakuyimbirani nyimbo pa zeze wa nsambo khumi,
To you, O God, I will sing a new song. On the psaltery, with an instrument of ten strings, I will sing psalms to you.
10 kwa Iye amene amapambanitsa mafumu, amene amapulumutsa Davide mtumiki wake ku lupanga loopsa.
He gives salvation to kings. He has redeemed your servant David from the malignant sword.
11 Landitseni ndi kundipulumutsa, mʼmanja mwa anthu achilendo, amene pakamwa pawo ndi podzaza ndi mabodza, amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.
Rescue me, and deliver me from the hand of the sons of foreigners. Their mouth has been speaking vain things, and their right hand is the right hand of iniquity.
12 Ndipo ana aamuna pa chinyamata chawo adzakhala ngati mbewu yosamalidwa bwino, ana athu aakazi adzakhala ngati zipilala zosemedwa bwino, zokongoletsera nyumba yaufumu.
Their sons are like new plantings in their youth. Their daughters are dressed up: adorned all around like the idols of a temple.
13 Nkhokwe zathu zidzakhala zodzaza ndi zokolola za mtundu uliwonse. Nkhosa zathu zidzaswana miyandamiyanda pa mabusa athu.
Their cupboards are full: overflowing from one thing into another. Their sheep bear young, brought forth in abundance.
14 Ngʼombe zathu zidzanyamula katundu wolemera. Sipadzakhala mingʼalu pa makoma, sipadzakhalanso kupita ku ukapolo, mʼmisewu mwathu simudzakhala kulira chifukwa cha mavuto.
Their cattle are fat. There is no ruined wall or passage, nor anyone crying out in their streets.
15 Odala anthu amene adzalandira madalitso awa; odala anthu amene Mulungu wawo ndi Yehova.
They have called the people that has these things: blessed. But blessed is the people whose God is the Lord.

< Masalimo 144 >