< Masalimo 143 >

1 Salimo la Davide. Yehova imvani pemphero langa, mvetserani kulira kwanga kopempha chifundo; mwa kukhulupirika kwanu ndi chilungamo chanu bwerani kudzandithandiza.
Psaume de David. Seigneur, écoute ma prière, prête l’oreille à mes supplications, dans ta fidélité réponds-moi, et dans ta bienveillance:
2 Musazenge mlandu mtumiki wanu, pakuti palibe munthu wamoyo amene ndi wolungama pamaso panu.
n’entre pas en jugement avec ton serviteur, car nul vivant ne peut se trouver juste à tes yeux.
3 Mdani akundithamangitsa, iye wandipondereza pansi; wachititsa kuti ndikhale mu mdima ngati munthu amene anafa kale.
C’Est que l’ennemi s’est jeté à ma poursuite, a broyé ma vie sur le sol, me plongeant dans les ténèbres, comme ceux qui, dès longtemps, appartiennent à la mort.
4 Choncho mzimu wanga ukufowoka mʼkati mwanga; mʼkati mwanga, mtima wanga uli ndi nkhawa.
Mon esprit tombe en défaillance en moi, en mon sein mon cœur est frappé de stupeur.
5 Ndimakumbukira masiku amakedzana; ndimalingalira za ntchito yanu yonse, ndimaganizira zimene manja anu anachita.
J’Évoque le souvenir des jours antiques, je pense à l’ensemble de tes actes, et médite sur l’œuvre de tes mains.
6 Ndatambalitsa manja anga kwa Inu; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu monga nthaka yowuma. (Sela)
Je tends les mains vers toi; mon âme, telle une terre aride, a soif de toi. (Sélah)
7 Yehova ndiyankheni msanga; mzimu wanga ukufowoka. Musandibisire nkhope yanu, mwina ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
Sans retard exauce-moi, ô Seigneur, mon esprit se consume; ne me dérobe point ta face, sinon je ressemblerai à ceux qui descendent dans la tombe.
8 Lolani kuti mmawa ubweretse mawu achikondi chanu chosasinthika, pakuti ine ndimadalira Inu. Mundisonyeze njira yoti ndiyendemo, pakuti kwa Inu nditukulira moyo wanga.
Dès le matin, annonce-moi ta grâce, car j’ai mis confiance en toi; fais-moi connaître le chemin que je dois suivre, car vers toi j’élève mon âme.
9 Pulumutseni kwa adani anga, Inu Yehova, pakuti ndimabisala mwa Inu.
Délivre-moi de mes ennemis, Eternel, c’est en toi que je cherche un abri,
10 Phunzitseni kuchita chifuniro chanu, popeza ndinu Mulungu wanga; Mzimu wanu wabwino unditsogolere pa njira yanu yosalala.
Enseigne-moi à accomplir ta volonté, car c’est toi qui es mon Dieu; que ton esprit bienveillant me guide sur un sol uni!
11 Sungani moyo wanga Inu Yehova chifukwa cha dzina lanu; mwa chilungamo chanu tulutseni mʼmasautso anga.
En faveur de ton nom, Eternel, tu me conserveras en vie; dans ta justice, tu libéreras mon âme de la détresse.
12 Mwa chikondi chanu chosasinthika khalitsani chete adani anga; wonongani adani anga, pakuti ndine mtumiki wanu.
Dans ta bonté, tu anéantiras mes ennemis, tu feras périr tous ceux qui me sont hostiles, car je suis ton serviteur.

< Masalimo 143 >