< Masalimo 143 >

1 Salimo la Davide. Yehova imvani pemphero langa, mvetserani kulira kwanga kopempha chifundo; mwa kukhulupirika kwanu ndi chilungamo chanu bwerani kudzandithandiza.
Psaume de David. Éternel! écoute ma prière; prête l’oreille à mes supplications; dans ta fidélité réponds-moi dans ta justice.
2 Musazenge mlandu mtumiki wanu, pakuti palibe munthu wamoyo amene ndi wolungama pamaso panu.
Et n’entre pas en jugement avec ton serviteur, car devant toi nul homme vivant ne sera justifié.
3 Mdani akundithamangitsa, iye wandipondereza pansi; wachititsa kuti ndikhale mu mdima ngati munthu amene anafa kale.
Car l’ennemi poursuit mon âme, il foule ma vie par terre; il me fait habiter dans des lieux ténébreux, comme ceux qui sont morts depuis longtemps.
4 Choncho mzimu wanga ukufowoka mʼkati mwanga; mʼkati mwanga, mtima wanga uli ndi nkhawa.
Et mon esprit est accablé en moi, mon cœur est désolé au-dedans de moi.
5 Ndimakumbukira masiku amakedzana; ndimalingalira za ntchito yanu yonse, ndimaganizira zimene manja anu anachita.
Je me souviens des jours d’autrefois, je pense à tous tes actes, je médite les œuvres de tes mains.
6 Ndatambalitsa manja anga kwa Inu; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu monga nthaka yowuma. (Sela)
J’étends mes mains vers toi; mon âme, comme une terre altérée, [a soif] de toi. (Sélah)
7 Yehova ndiyankheni msanga; mzimu wanga ukufowoka. Musandibisire nkhope yanu, mwina ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
Éternel! hâte-toi, réponds-moi! mon esprit défaille en moi. Ne me cache pas ta face! autrement je serai semblable à ceux qui descendent dans la fosse.
8 Lolani kuti mmawa ubweretse mawu achikondi chanu chosasinthika, pakuti ine ndimadalira Inu. Mundisonyeze njira yoti ndiyendemo, pakuti kwa Inu nditukulira moyo wanga.
Fais-moi entendre dès le matin ta bonté, car en toi j’ai mis ma confiance; fais-moi connaître le chemin où j’ai à marcher, car c’est à toi que j’élève mon âme.
9 Pulumutseni kwa adani anga, Inu Yehova, pakuti ndimabisala mwa Inu.
Éternel! délivre-moi de mes ennemis! c’est vers toi que je me réfugie.
10 Phunzitseni kuchita chifuniro chanu, popeza ndinu Mulungu wanga; Mzimu wanu wabwino unditsogolere pa njira yanu yosalala.
Enseigne-moi à faire ce qui te plaît, car tu es mon Dieu; que ton bon Esprit me conduise dans un pays uni.
11 Sungani moyo wanga Inu Yehova chifukwa cha dzina lanu; mwa chilungamo chanu tulutseni mʼmasautso anga.
À cause de ton nom, ô Éternel! fais-moi vivre; dans ta justice, fais sortir mon âme de la détresse,
12 Mwa chikondi chanu chosasinthika khalitsani chete adani anga; wonongani adani anga, pakuti ndine mtumiki wanu.
Et, dans ta bonté, extermine mes ennemis, et détruis tous ceux qui oppriment mon âme; car je suis ton serviteur.

< Masalimo 143 >