< Masalimo 143 >

1 Salimo la Davide. Yehova imvani pemphero langa, mvetserani kulira kwanga kopempha chifundo; mwa kukhulupirika kwanu ndi chilungamo chanu bwerani kudzandithandiza.
Psaume de David. Yahweh, écoute ma prière; prête l’oreille à mes supplications; exauce-moi dans ta vérité et dans ta justice.
2 Musazenge mlandu mtumiki wanu, pakuti palibe munthu wamoyo amene ndi wolungama pamaso panu.
N’entre pas en jugement avec ton serviteur, car aucun homme vivant n’est juste devant toi.
3 Mdani akundithamangitsa, iye wandipondereza pansi; wachititsa kuti ndikhale mu mdima ngati munthu amene anafa kale.
L’ennemi en veut à mon âme, il foule à terre ma vie; il me relègue dans les lieux ténébreux, comme ceux qui sont morts depuis longtemps.
4 Choncho mzimu wanga ukufowoka mʼkati mwanga; mʼkati mwanga, mtima wanga uli ndi nkhawa.
Mon esprit défaille en moi, mon cœur est troublé dans mon sein.
5 Ndimakumbukira masiku amakedzana; ndimalingalira za ntchito yanu yonse, ndimaganizira zimene manja anu anachita.
Je pense aux jours d’autrefois, je médite sur toutes tes œuvres, je réfléchis sur l’ouvrage de tes mains.
6 Ndatambalitsa manja anga kwa Inu; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu monga nthaka yowuma. (Sela)
j’étends vers toi mes mains, et mon âme, comme une terre desséchée, soupire après toi. — Séla.
7 Yehova ndiyankheni msanga; mzimu wanga ukufowoka. Musandibisire nkhope yanu, mwina ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
Hâte-toi de m’exaucer, Yahweh, mon esprit défaille; ne me cache pas ta face, je deviens semblable à ceux qui descendent dans la fosse.
8 Lolani kuti mmawa ubweretse mawu achikondi chanu chosasinthika, pakuti ine ndimadalira Inu. Mundisonyeze njira yoti ndiyendemo, pakuti kwa Inu nditukulira moyo wanga.
Fais-moi de bonne heure sentir ta bonté, car c’est en toi que j’espère; fais-moi connaître la voie où je dois marcher, car c’est vers toi que j’élève mon âme.
9 Pulumutseni kwa adani anga, Inu Yehova, pakuti ndimabisala mwa Inu.
Délivre-moi de mes ennemis, Yahweh, je me réfugie auprès de toi.
10 Phunzitseni kuchita chifuniro chanu, popeza ndinu Mulungu wanga; Mzimu wanu wabwino unditsogolere pa njira yanu yosalala.
Apprends-moi à faire ta volonté, car tu es mon Dieu. Que ton bon esprit me conduise dans la voie droite!
11 Sungani moyo wanga Inu Yehova chifukwa cha dzina lanu; mwa chilungamo chanu tulutseni mʼmasautso anga.
A cause de ton nom, Yahweh, rends-moi la vie; dans ta justice, retire mon âme de la détresse.
12 Mwa chikondi chanu chosasinthika khalitsani chete adani anga; wonongani adani anga, pakuti ndine mtumiki wanu.
Dans ta bonté, anéantis mes ennemis, et fais périr tous ceux qui m’oppriment, car je suis ton serviteur.

< Masalimo 143 >