< Masalimo 143 >

1 Salimo la Davide. Yehova imvani pemphero langa, mvetserani kulira kwanga kopempha chifundo; mwa kukhulupirika kwanu ndi chilungamo chanu bwerani kudzandithandiza.
Y Salmon David. JUNGOG y tinayuyutto, O Jeova; ecungog y guinagaojo sija: opeyo pot y minagajetmo yan y tininasmo.
2 Musazenge mlandu mtumiki wanu, pakuti palibe munthu wamoyo amene ndi wolungama pamaso panu.
Ya chamo jumajalom gui juisio yan y tentagomo: sa taya taotao lalâlâ umajustifica gui menamo.
3 Mdani akundithamangitsa, iye wandipondereza pansi; wachititsa kuti ndikhale mu mdima ngati munthu amene anafa kale.
Sa y enimigo guinin japetsigue y antijo; guinin jasaulag papa gui jilo oda y jaanijo: janasagayo gui anae jomjom na lugat sija, taegüije sija y guinin apmam na manmatae.
4 Choncho mzimu wanga ukufowoka mʼkati mwanga; mʼkati mwanga, mtima wanga uli ndi nkhawa.
Enaomina y espiritujo, lalango gui sumanjalomjo: y corasonjo gui sumanjalomjo triste.
5 Ndimakumbukira masiku amakedzana; ndimalingalira za ntchito yanu yonse, ndimaganizira zimene manja anu anachita.
Jujaso sija y apmam na jaane; jujaso todo y chechomo; jujajaso y checho y canaemo.
6 Ndatambalitsa manja anga kwa Inu; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu monga nthaka yowuma. (Sela)
Jujuto mona y canaejo guiya jago: y antijo majo nu jago, taegüije y anglo na tano. (Sila)
7 Yehova ndiyankheni msanga; mzimu wanga ukufowoka. Musandibisire nkhope yanu, mwina ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
Jungogyo enseguidas, O Jeova: sa malayo y antijo: chamo na naaatog y matamo guiya guajo; sa noseaja juparejo yan ayo sija y mannunog gui jalom joyo.
8 Lolani kuti mmawa ubweretse mawu achikondi chanu chosasinthika, pakuti ine ndimadalira Inu. Mundisonyeze njira yoti ndiyendemo, pakuti kwa Inu nditukulira moyo wanga.
Na jungogyo ni y cariñoso na güinaeyamo gui egaan; sa jagoja nae juangocoyo: natungoyo ni y chalan anae para jufamocat; sa jujatsa julo y antijo guiya jago.
9 Pulumutseni kwa adani anga, Inu Yehova, pakuti ndimabisala mwa Inu.
Nalibreyo, O Jeova, gui enemigujo sija: jufalagüe jao, ya unnaatogyo.
10 Phunzitseni kuchita chifuniro chanu, popeza ndinu Mulungu wanga; Mzimu wanu wabwino unditsogolere pa njira yanu yosalala.
Fanagüeyo ya jufatinas y minalagomo: sa jago y Yuusso: y espiritumo mauleg; osgaejonyo gui tano y manunas.
11 Sungani moyo wanga Inu Yehova chifukwa cha dzina lanu; mwa chilungamo chanu tulutseni mʼmasautso anga.
Nalâlâyo, O Jeova, pot y naanmo: pot y tininasmo, chule y antijo gui chinatsaga.
12 Mwa chikondi chanu chosasinthika khalitsani chete adani anga; wonongani adani anga, pakuti ndine mtumiki wanu.
Yan pot y cariñoso na güinaeyamo utut y enemigujo sija, ya unyulang todo sija y munapinite y antijo: sa guajo tentagomo.

< Masalimo 143 >