< Masalimo 141 >

1 Salimo la Davide. Inu Yehova ndikukuyitanani; bwerani msanga kwa ine. Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu.
En Psalm Davids. Herre, jag ropar till dig, skynda dig till mig. Förnim mina röst, när jag åkallar dig.
2 Pemphero langa lifike kwa Inu ngati lubani; kukweza manja kwanga kukhale ngati nsembe yamadzulo.
Min bön gälle inför dig såsom ett rökoffer; mina händers upphäfvande, såsom ett aftonoffer.
3 Yehova ikani mlonda pakamwa panga; londerani khomo la pa milomo yanga.
Herre, bevara min mun, och bevara mina läppar.
4 Musalole kuti mtima wanga ukokedwere ku zoyipa; kuchita ntchito zonyansa pamodzi ndi anthu amene amachita zoyipa; musalole kuti ndidye nawo zokoma zawo.
Böj icke mitt hjerta till något det ondt är, till att föra ett ogudaktigt väsende med de ogerningsmän; att jag icke äter af det som dem lyster.
5 Munthu wolungama andikanthe, chimenecho ndiye chifundo; andidzudzule ndiye mafuta pa mutu wanga. Mutu wanga sudzakana zimenezi. Komabe pemphero langa nthawi zonse ndi lotsutsana ndi ntchito za anthu ochita zoyipa.
Den rättfärdige slå mig vänliga, och straffe mig. Det skall göra mig så godt, som balsam på mitt hufvud; ty jag beder städse, att de icke skola göra mig skada.
6 Olamulira awo adzaponyedwa pansi kuchokera pa malo okwera kwambiri, ndipo anthu oyipa adzaphunzira kuti mawu anga anayankhulidwa bwino.
Deras lärare störte öfver en sten; så skall man då sedan höra mina läro, att hon lustig är.
7 Iwo adzati, “Monga momwe nkhuni zimamwazikira akaziwaza, ndi momwenso mafupa athu amwazikira pa khomo la manda.” (Sheol h7585)
Vår ben äro förströdd allt intill helvetet, såsom då en upprifver och uppkastar jordena. (Sheol h7585)
8 Koma maso anga akupenyetsetsa Inu Ambuye Wamphamvuzonse; ndimathawira kwa Inu, musandipereke ku imfa.
Ty uppå dig, Herre, Herre, se min ögon. Jag tröster uppå dig; bortkasta icke mina själ.
9 Mundipulumutse ku misampha imene anditchera, ku makhwekhwe amene anthu oyipa andikonzera.
Bevara mig för den snaro, som de mig satt hafva, och för de ogerningsmäns gildre.
10 Anthu oyipa akodwe mʼmaukonde awo, mpaka ine nditadutsa mwamtendere.
De ogudaktige falle med hvarannan uti sina egna nät; men jag gånge alltid framom.

< Masalimo 141 >