< Masalimo 141 >

1 Salimo la Davide. Inu Yehova ndikukuyitanani; bwerani msanga kwa ine. Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu.
A psalm of David. Yahweh, I am crying out to you; come quickly to me. Listen to me when I call to you.
2 Pemphero langa lifike kwa Inu ngati lubani; kukweza manja kwanga kukhale ngati nsembe yamadzulo.
May my prayer be like incense before you; may my lifted hands be like the evening sacrifice.
3 Yehova ikani mlonda pakamwa panga; londerani khomo la pa milomo yanga.
Yahweh, place a guard over my mouth; guard the door of my lips.
4 Musalole kuti mtima wanga ukokedwere ku zoyipa; kuchita ntchito zonyansa pamodzi ndi anthu amene amachita zoyipa; musalole kuti ndidye nawo zokoma zawo.
Do not let my heart desire any evil thing or participate in sinful activities with men who behave wickedly. May I not eat any of their delicacies.
5 Munthu wolungama andikanthe, chimenecho ndiye chifundo; andidzudzule ndiye mafuta pa mutu wanga. Mutu wanga sudzakana zimenezi. Komabe pemphero langa nthawi zonse ndi lotsutsana ndi ntchito za anthu ochita zoyipa.
Let a righteous man hit me; it will be a kindness to me. Let him correct me; it will be like oil on my head; may my head not refuse to accept it. But my prayer is always against their wicked deeds.
6 Olamulira awo adzaponyedwa pansi kuchokera pa malo okwera kwambiri, ndipo anthu oyipa adzaphunzira kuti mawu anga anayankhulidwa bwino.
Their leaders will be thrown down from the top of cliffs; they will hear that my own words are pleasant.
7 Iwo adzati, “Monga momwe nkhuni zimamwazikira akaziwaza, ndi momwenso mafupa athu amwazikira pa khomo la manda.” (Sheol h7585)
They will have to say, “As when one plows and breaks up the ground, so our bones have been scattered at the mouth of Sheol.” (Sheol h7585)
8 Koma maso anga akupenyetsetsa Inu Ambuye Wamphamvuzonse; ndimathawira kwa Inu, musandipereke ku imfa.
Surely my eyes are on you, Yahweh, Lord; in you I take refuge; do not leave my soul defenseless.
9 Mundipulumutse ku misampha imene anditchera, ku makhwekhwe amene anthu oyipa andikonzera.
Protect me from the snares that they have laid for me, from the traps of evildoers.
10 Anthu oyipa akodwe mʼmaukonde awo, mpaka ine nditadutsa mwamtendere.
Let the wicked fall into their own nets while I escape.

< Masalimo 141 >