< Masalimo 141 >
1 Salimo la Davide. Inu Yehova ndikukuyitanani; bwerani msanga kwa ine. Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu.
“For the leader of the music. A psalm of David.” I cry to thee, O LORD! make haste unto me! Give ear to my voice, when I cry unto thee!
2 Pemphero langa lifike kwa Inu ngati lubani; kukweza manja kwanga kukhale ngati nsembe yamadzulo.
Let my prayer come before thee as incense, And the lifting-up of my hands, as the evening sacrifice!
3 Yehova ikani mlonda pakamwa panga; londerani khomo la pa milomo yanga.
Set a watch, O LORD! before my mouth; Guard the door of my lips!
4 Musalole kuti mtima wanga ukokedwere ku zoyipa; kuchita ntchito zonyansa pamodzi ndi anthu amene amachita zoyipa; musalole kuti ndidye nawo zokoma zawo.
Let not my heart incline to any evil thing; Let me not practise wickedness with the doers of iniquity, And let me not eat of their delicacies!
5 Munthu wolungama andikanthe, chimenecho ndiye chifundo; andidzudzule ndiye mafuta pa mutu wanga. Mutu wanga sudzakana zimenezi. Komabe pemphero langa nthawi zonse ndi lotsutsana ndi ntchito za anthu ochita zoyipa.
Let the righteous smite me, —it shall be a kindness; Let him reprove me, and it shall be oil for my head; Let him do it again, and my head shall not refuse it; But now I pray against their wickedness!
6 Olamulira awo adzaponyedwa pansi kuchokera pa malo okwera kwambiri, ndipo anthu oyipa adzaphunzira kuti mawu anga anayankhulidwa bwino.
When their judges are hurled over the side of the rock, They shall hear how pleasant are my words.
7 Iwo adzati, “Monga momwe nkhuni zimamwazikira akaziwaza, ndi momwenso mafupa athu amwazikira pa khomo la manda.” (Sheol )
So are our bones scattered at the mouth of the underworld, As when one furroweth and ploweth up the land. (Sheol )
8 Koma maso anga akupenyetsetsa Inu Ambuye Wamphamvuzonse; ndimathawira kwa Inu, musandipereke ku imfa.
But to thee do my eyes look, O Lord Jehovah! In thee is my trust; Let not my life be poured out!
9 Mundipulumutse ku misampha imene anditchera, ku makhwekhwe amene anthu oyipa andikonzera.
Preserve me from the snares which they have laid for me, And from the nets of evil-doers!
10 Anthu oyipa akodwe mʼmaukonde awo, mpaka ine nditadutsa mwamtendere.
Let the wicked fall together into their own traps, Whilst I make my escape!