< Masalimo 140 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Landitseni Yehova kwa anthu oyipa; tetezeni kwa anthu ankhanza,
Salmo de Davi, para o regente: Livra-me do homem mau, SENHOR; guarda-me dos homens violentos,
2 amene mu mtima mwawo amakonza zinthu zoyipa ndi kuyambitsa nkhondo tsiku lililonse.
Que pensam maldades no coração; todo dia se reúnem para fazerem guerra.
3 Iwo amanola malilime awo kukhala akuthwa ngati a njoka; pa milomo yawo pali ululu wa mamba. (Sela)
Eles afiam suas línguas como a cobra; veneno de serpentes [há] debaixo de seus lábios. (Selá)
4 Tetezeni Inu Yehova, kwa anthu oyipa; tchinjirizeni kwa anthu ankhanza amene amakonza zokola mapazi anga.
Guarda-me, SENHOR, das mãos do perverso; guarda-me do homens violentos, que pensam em empurrar os meus pés.
5 Anthu odzikuza anditchera msampha mobisika; iwo atchera zingwe za maukonde awo ndipo anditchera misampha pa njira yanga. (Sela)
Os arrogantes me armaram ciladas e cordas; estenderam uma rede de um lado do caminho; [e] puseram laços de armadilhas para mim. (Selá)
6 Inu Yehova, ine ndikuti, “Ndinu Mulungu wanga.” Imvani kupempha kwanga Yehova.
Eu disse ao SENHOR: Tu [és] meu Deus; inclina teus ouvidos à voz de minhas súplicas, SENHOR.
7 Inu Ambuye Wamphamvuzonse, Mpulumutsi wanga wamphamvu, mumateteza mutu wanga tsiku lankhondo.
Ó Senhor DEUS, força de minha salvação, cobriste minha cabeça no dia da batalha.
8 Musawapatse anthu oyipa zokhumba zawo, Inu Yehova; musalole kuti zokonza zawo zitheke, mwina iwo adzayamba kunyada. (Sela)
Não concedas ao perverso os desejos dele, SENHOR; não permitas suceder seu plano maligno, [pois senão] se exaltariam. (Selá)
9 Mitu ya amene andizungulira iphimbidwe ndi masautso amene milomo yawo yayambitsa.
Quanto à cabeça dos que me cercam, que a opressão de seus próprios lábios os cubra.
10 Makala amoto agwere pa iwo; aponyedwe pa moto, mʼmaenje amatope, asatulukemonso.
Caiam sobre eles brasas vivas; faça-os cair no fogo [e] em covas profundas, [para que] não se levantem mais.
11 Musalole kuti anthu achipongwe akhazikike mʼdziko; choyipa chilondole anthu ankhanza.
O homem de língua maligna não se firmará na terra; o mal perseguirá o homem violento até o derrubar.
12 Ndikudziwa kuti Yehova amapereka chiweruzo cholungama kwa anthu osauka, ndipo amateteza zolinga za anthu osowa.
Eu sei que o SENHOR cumprirá a causa do aflito, o direito dos necessitados.
13 Zoonadi anthu olungama adzatamanda dzina lanu, ndipo anthu owongoka mtima adzakhala pamaso panu.
Certamente os justos agradecerão ao teu nome; os corretos habitarão perante teu rosto.