< Masalimo 140 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Landitseni Yehova kwa anthu oyipa; tetezeni kwa anthu ankhanza,
Pour la fin, psaume de David. Arrachez-moi, Seigneur, à l’homme méchant: à l’homme inique arrachez-moi.
2 amene mu mtima mwawo amakonza zinthu zoyipa ndi kuyambitsa nkhondo tsiku lililonse.
Ceux qui ont pensé des iniquités dans leur cœur, durant tout le jour préparaient des combats.
3 Iwo amanola malilime awo kukhala akuthwa ngati a njoka; pa milomo yawo pali ululu wa mamba. (Sela)
Ils ont aiguisé leur langue comme celle d’un serpent: le venin d’un aspic est sous leurs lèvres.
4 Tetezeni Inu Yehova, kwa anthu oyipa; tchinjirizeni kwa anthu ankhanza amene amakonza zokola mapazi anga.
Gardez-moi, Seigneur, de la main d’un pécheur, et arrachez-moi à des hommes iniques. Ils ont pensé à ébranler mes pas;
5 Anthu odzikuza anditchera msampha mobisika; iwo atchera zingwe za maukonde awo ndipo anditchera misampha pa njira yanga. (Sela)
Des hommes superbes ont caché un lacs devant moi: Et ils ont tendu des cordes en lacs, le long du chemin ils ont posé une pierre d’achoppement devant moi.
6 Inu Yehova, ine ndikuti, “Ndinu Mulungu wanga.” Imvani kupempha kwanga Yehova.
J’ai dit au Seigneur: C’est vous qui êtes mon Dieu; exaucez, Seigneur, la voix de ma supplication.
7 Inu Ambuye Wamphamvuzonse, Mpulumutsi wanga wamphamvu, mumateteza mutu wanga tsiku lankhondo.
Seigneur, Seigneur, la force de mon salut, vous avez couvert ma tête de votre ombre au jour du combat;
8 Musawapatse anthu oyipa zokhumba zawo, Inu Yehova; musalole kuti zokonza zawo zitheke, mwina iwo adzayamba kunyada. (Sela)
Ne me livrez pas, Seigneur, à un pécheur contre mon désir: ils ont conspiré contre moi, ne me délaissez pas, de peur qu’ils ne triomphent.
9 Mitu ya amene andizungulira iphimbidwe ndi masautso amene milomo yawo yayambitsa.
La tête de leur circuit, le travail de leurs lèvres les couvrira eux-mêmes.
10 Makala amoto agwere pa iwo; aponyedwe pa moto, mʼmaenje amatope, asatulukemonso.
Des charbons tomberont sur eux, vous les précipiterez dans le feu: dans leurs misères, ils ne subsisteront pas.
11 Musalole kuti anthu achipongwe akhazikike mʼdziko; choyipa chilondole anthu ankhanza.
Un homme à la langue méchante ne sera pas dirigé sur la terre: les maux saisiront un homme injuste à la mort.
12 Ndikudziwa kuti Yehova amapereka chiweruzo cholungama kwa anthu osauka, ndipo amateteza zolinga za anthu osowa.
Je sais que le Seigneur se chargera de la cause de l’homme sans secours, et de la vengeance des pauvres.
13 Zoonadi anthu olungama adzatamanda dzina lanu, ndipo anthu owongoka mtima adzakhala pamaso panu.
Cependant les justes glorifieront votre nom; et les hommes droits vivront avec vous.