< Masalimo 140 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Landitseni Yehova kwa anthu oyipa; tetezeni kwa anthu ankhanza,
To victorie, the salm of Dauith. Lord, delyuere thou me fro an yuel man; delyuere thou me fro a wickid man.
2 amene mu mtima mwawo amakonza zinthu zoyipa ndi kuyambitsa nkhondo tsiku lililonse.
Whiche thouyten wickidnesses in the herte; al dai thei ordeyneden batels.
3 Iwo amanola malilime awo kukhala akuthwa ngati a njoka; pa milomo yawo pali ululu wa mamba. (Sela)
Thei scharpiden her tungis as serpentis; the venym of snakis vndir the lippis of hem.
4 Tetezeni Inu Yehova, kwa anthu oyipa; tchinjirizeni kwa anthu ankhanza amene amakonza zokola mapazi anga.
Lord, kepe thou me fro the hond of the synnere; and delyuere thou me fro wickid men. Which thouyten to disseyue my goyngis;
5 Anthu odzikuza anditchera msampha mobisika; iwo atchera zingwe za maukonde awo ndipo anditchera misampha pa njira yanga. (Sela)
proude men hidden a snare to me. And thei leiden forth cordis in to a snare; thei settiden sclaundir to me bisidis the weie.
6 Inu Yehova, ine ndikuti, “Ndinu Mulungu wanga.” Imvani kupempha kwanga Yehova.
I seide to the Lord, Thou art mi God; Lord, here thou the vois of my biseching.
7 Inu Ambuye Wamphamvuzonse, Mpulumutsi wanga wamphamvu, mumateteza mutu wanga tsiku lankhondo.
Lord, Lord, the vertu of myn heelthe; thou madist schadowe on myn heed in the dai of batel.
8 Musawapatse anthu oyipa zokhumba zawo, Inu Yehova; musalole kuti zokonza zawo zitheke, mwina iwo adzayamba kunyada. (Sela)
Lord, bitake thou not me fro my desire to the synnere; thei thouyten ayens me, forsake thou not me, lest perauenture thei ben enhaunsid.
9 Mitu ya amene andizungulira iphimbidwe ndi masautso amene milomo yawo yayambitsa.
The heed of the cumpas of hem; the trauel of her lippis schal hile hem.
10 Makala amoto agwere pa iwo; aponyedwe pa moto, mʼmaenje amatope, asatulukemonso.
Colis schulen falle on hem, thou schalt caste hem doun in to fier; in wretchidnessis thei schulen not stonde.
11 Musalole kuti anthu achipongwe akhazikike mʼdziko; choyipa chilondole anthu ankhanza.
A man a greet ianglere schal not be dressid in erthe; yuels schulen take an vniust man in perisching.
12 Ndikudziwa kuti Yehova amapereka chiweruzo cholungama kwa anthu osauka, ndipo amateteza zolinga za anthu osowa.
I haue knowe, that the Lord schal make dom of a nedi man; and the veniaunce of pore men.
13 Zoonadi anthu olungama adzatamanda dzina lanu, ndipo anthu owongoka mtima adzakhala pamaso panu.
Netheles iust men schulen knouleche to thi name; and riytful men schulen dwelle with thi cheer.

< Masalimo 140 >