< Masalimo 140 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Landitseni Yehova kwa anthu oyipa; tetezeni kwa anthu ankhanza,
To the chief Musician, A Psalm of David. Deliver me, O LORD, from the evil man: preserve me from the violent man;
2 amene mu mtima mwawo amakonza zinthu zoyipa ndi kuyambitsa nkhondo tsiku lililonse.
Who imagine mischiefs in their heart; continually are they gathered together for war.
3 Iwo amanola malilime awo kukhala akuthwa ngati a njoka; pa milomo yawo pali ululu wa mamba. (Sela)
They have sharpened their tongues like a serpent; adders’ poison is under their lips. (Selah)
4 Tetezeni Inu Yehova, kwa anthu oyipa; tchinjirizeni kwa anthu ankhanza amene amakonza zokola mapazi anga.
Keep me, O LORD, from the hands of the wicked; preserve me from the violent man; who have purposed to overthrow my goings.
5 Anthu odzikuza anditchera msampha mobisika; iwo atchera zingwe za maukonde awo ndipo anditchera misampha pa njira yanga. (Sela)
The proud have hid a trap for me, and cords; they have spread a net by the way side; they have set snares for me. (Selah)
6 Inu Yehova, ine ndikuti, “Ndinu Mulungu wanga.” Imvani kupempha kwanga Yehova.
I said to the LORD, Thou art my God: hear the voice of my supplications, O LORD.
7 Inu Ambuye Wamphamvuzonse, Mpulumutsi wanga wamphamvu, mumateteza mutu wanga tsiku lankhondo.
O GOD the Lord, the strength of my salvation, thou hast covered my head in the day of battle.
8 Musawapatse anthu oyipa zokhumba zawo, Inu Yehova; musalole kuti zokonza zawo zitheke, mwina iwo adzayamba kunyada. (Sela)
Grant not, O LORD, the desires of the wicked: further not his wicked device; lest they exalt themselves. (Selah)
9 Mitu ya amene andizungulira iphimbidwe ndi masautso amene milomo yawo yayambitsa.
As for the head of those that surroundeth me, let the mischief of their own lips cover them.
10 Makala amoto agwere pa iwo; aponyedwe pa moto, mʼmaenje amatope, asatulukemonso.
Let burning coals fall upon them: let them be cast into the fire; into deep pits, that they rise not again.
11 Musalole kuti anthu achipongwe akhazikike mʼdziko; choyipa chilondole anthu ankhanza.
Let not an evil speaker be established on the earth: evil shall hunt the violent man to overthrow him.
12 Ndikudziwa kuti Yehova amapereka chiweruzo cholungama kwa anthu osauka, ndipo amateteza zolinga za anthu osowa.
I know that the LORD will maintain the cause of the afflicted, and the right of the poor.
13 Zoonadi anthu olungama adzatamanda dzina lanu, ndipo anthu owongoka mtima adzakhala pamaso panu.
Surely the righteous shall give thanks to thy name: the upright shall dwell in thy presence.

< Masalimo 140 >