< Masalimo 140 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Landitseni Yehova kwa anthu oyipa; tetezeni kwa anthu ankhanza,
For the music director. A psalm of David. Lord, please save me from those who do evil; protect me especially from those who are violent!
2 amene mu mtima mwawo amakonza zinthu zoyipa ndi kuyambitsa nkhondo tsiku lililonse.
Their minds are busy plotting evil things, stirring up trouble all day long.
3 Iwo amanola malilime awo kukhala akuthwa ngati a njoka; pa milomo yawo pali ululu wa mamba. (Sela)
Their tongues are as sharp as those of snakes; viper's venom is on their lips. (Selah)
4 Tetezeni Inu Yehova, kwa anthu oyipa; tchinjirizeni kwa anthu ankhanza amene amakonza zokola mapazi anga.
Lord, please keep me from falling into the hands of the wicked; protect me especially from those who are violent, who are plotting my downfall.
5 Anthu odzikuza anditchera msampha mobisika; iwo atchera zingwe za maukonde awo ndipo anditchera misampha pa njira yanga. (Sela)
Proud people have hidden a trap for me—they have strung out a net on the path, they have set snares to catch me. (Selah)
6 Inu Yehova, ine ndikuti, “Ndinu Mulungu wanga.” Imvani kupempha kwanga Yehova.
I told the Lord, “You are my God! Lord, please listen to my cries for help!”
7 Inu Ambuye Wamphamvuzonse, Mpulumutsi wanga wamphamvu, mumateteza mutu wanga tsiku lankhondo.
Lord God, my powerful Savior, you covered my head like a helmet on the day of battle.
8 Musawapatse anthu oyipa zokhumba zawo, Inu Yehova; musalole kuti zokonza zawo zitheke, mwina iwo adzayamba kunyada. (Sela)
God, don't allow the wicked to get what they want—don't let them be successful in what they plan so they don't become proud. (Selah)
9 Mitu ya amene andizungulira iphimbidwe ndi masautso amene milomo yawo yayambitsa.
May the harm spoken against me by those who surround me fall back on them,
10 Makala amoto agwere pa iwo; aponyedwe pa moto, mʼmaenje amatope, asatulukemonso.
Let burning coals rain down on them! Let them be thrown into the fire, or into bottomless pits, never to rise again.
11 Musalole kuti anthu achipongwe akhazikike mʼdziko; choyipa chilondole anthu ankhanza.
Don't let people who slander others live in our land. May disaster strike down violent people.
12 Ndikudziwa kuti Yehova amapereka chiweruzo cholungama kwa anthu osauka, ndipo amateteza zolinga za anthu osowa.
Yet I know the Lord defends the rights of those who are persecuted, and gives justice to the poor.
13 Zoonadi anthu olungama adzatamanda dzina lanu, ndipo anthu owongoka mtima adzakhala pamaso panu.
Truly those who live right are thankful for the kind of person you are, and those who are honest will live in your presence.

< Masalimo 140 >