< Masalimo 140 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Landitseni Yehova kwa anthu oyipa; tetezeni kwa anthu ankhanza,
За първия певец. Давидов псалом. Избави ме, Господи, от нечестивия човек, Опази ме от насилник човек,
2 amene mu mtima mwawo amakonza zinthu zoyipa ndi kuyambitsa nkhondo tsiku lililonse.
Които измислюват зло в сърцето си, И всеки ден възбуждат боеве.
3 Iwo amanola malilime awo kukhala akuthwa ngati a njoka; pa milomo yawo pali ululu wa mamba. (Sela)
Изострюват езика си като на змия; Аспидова отрова има под устните им. (Села)
4 Tetezeni Inu Yehova, kwa anthu oyipa; tchinjirizeni kwa anthu ankhanza amene amakonza zokola mapazi anga.
Опази ме, Господи, от ръцете на нечестивия, Защити ме от насилник човек, Които възнамериха да ме направят да падна.
5 Anthu odzikuza anditchera msampha mobisika; iwo atchera zingwe za maukonde awo ndipo anditchera misampha pa njira yanga. (Sela)
Горделивите скриха клопка за мене. Поставиха примка за мене. (Села)
6 Inu Yehova, ine ndikuti, “Ndinu Mulungu wanga.” Imvani kupempha kwanga Yehova.
Рекох Господу: Ти си мой Бог; Послушай, Господи, гласа на молбите ми.
7 Inu Ambuye Wamphamvuzonse, Mpulumutsi wanga wamphamvu, mumateteza mutu wanga tsiku lankhondo.
Господи Боже, силний ми спасителю, Ти си покрил главата ми в ден на бой.
8 Musawapatse anthu oyipa zokhumba zawo, Inu Yehova; musalole kuti zokonza zawo zitheke, mwina iwo adzayamba kunyada. (Sela)
Господи, не удовлетворявай желанията на нечестивия; Не оставяй да успее злият му помисъл, Да не би да се надигат. (Села)
9 Mitu ya amene andizungulira iphimbidwe ndi masautso amene milomo yawo yayambitsa.
Нечестието на собствените им устни нека покрие главата На ония, които ме окръжават.
10 Makala amoto agwere pa iwo; aponyedwe pa moto, mʼmaenje amatope, asatulukemonso.
Разпалени въглища нека паднат върху тях; Нека бъдат хвърлени в огъня. В дълбоки води, за да не станат вече.
11 Musalole kuti anthu achipongwe akhazikike mʼdziko; choyipa chilondole anthu ankhanza.
Злоезичен човек няма да се утвърди на земята; Зло ще преследва насилника човек догдето го погуби.
12 Ndikudziwa kuti Yehova amapereka chiweruzo cholungama kwa anthu osauka, ndipo amateteza zolinga za anthu osowa.
Зная, че Господ ще защити делото на угнетения И правото на немотните.
13 Zoonadi anthu olungama adzatamanda dzina lanu, ndipo anthu owongoka mtima adzakhala pamaso panu.
Наистина праведните ще славят името Ти; Правдивите ще обитават пред лицето Ти.