< Masalimo 14 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Chitsiru chimati mu mtima mwake, “Kulibe Mulungu.” Oterewa ndi oyipa ndipo ntchito zawo ndi zonyansa; palibe amene amachita zabwino.
Psaume de David, [donné] au maître chantre. L'insensé a dit en son cœur: il n'y a point de Dieu. Ils se sont corrompus, ils se sont rendus abominables en leurs actions; il n'y a personne qui fasse le bien.
2 Yehova kumwamba wayangʼana pansi, kuyangʼana anthu onse kuti aone ngati alipo wina wanzeru, amene amafunafuna Mulungu.
L'Eternel a regardé des cieux sur les fils des hommes, pour voir s'il y en a quelqu'un qui soit intelligent, [et] qui cherche Dieu.
3 Onse atembenukira kumbali, onse pamodzi asanduka oyipa; palibe amene amachita zabwino, palibiretu ndi mmodzi yemwe.
Ils se sont tous égarés, ils se sont tous ensemble rendus odieux, il n'y a personne qui fasse le bien, non pas même un seul.
4 Kodi anthu ochita zoyipawa sadziwa chilichonse? Akudya anthu anga ngati chakudya chawo ndipo satamanda Yehova?
Tous ces ouvriers d'iniquité n'ont-ils point de connaissance? Ils mangent mon peuple [comme] s'ils mangeaient du pain, ils n'invoquent point l'Eternel.
5 Awo ali apowo, agwidwa ndi mantha aakulu, pakuti Mulungu ali mʼgulu la olungama.
Là ils seront saisis d'une grande frayeur; car Dieu est avec la race juste.
6 Inu ochita zoyipa mumalepheretsa chikonzero cha anthu osauka, koma Yehova ndiye pothawirapo pawo.
Vous faites honte à l'affligé de ce qu'il s'est proposé l'Eternel pour sa retraite.
7 Ndithu, chipulumutso cha Israeli chidzachokera ku Ziyoni! Pamene Yehova abwezeretsa ufulu wa anthu ake, Yakobo akondwere ndipo Israeli asangalale!
Ô! qui donnera de Sion la délivrance d'Israël! Quand l'Eternel aura ramené son peuple captif, Jacob s'égaiera, Israël se réjouira.

< Masalimo 14 >