< Masalimo 14 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Chitsiru chimati mu mtima mwake, “Kulibe Mulungu.” Oterewa ndi oyipa ndipo ntchito zawo ndi zonyansa; palibe amene amachita zabwino.
“For the leader of the music. A psalm of David.” The fool saith in his heart, “There is no God.” They are corrupt; abominable are their doings; There is none that doeth good.
2 Yehova kumwamba wayangʼana pansi, kuyangʼana anthu onse kuti aone ngati alipo wina wanzeru, amene amafunafuna Mulungu.
Jehovah looketh down from heaven upon the children of men, To see if there are any that have understanding, That have regard to God.
3 Onse atembenukira kumbali, onse pamodzi asanduka oyipa; palibe amene amachita zabwino, palibiretu ndi mmodzi yemwe.
They are all gone out of the way; together are they corrupt; There is none that doeth good—no, not one.
4 Kodi anthu ochita zoyipawa sadziwa chilichonse? Akudya anthu anga ngati chakudya chawo ndipo satamanda Yehova?
Shall not the evil-doers be requited, Who devour my people like bread, And call not upon Jehovah?
5 Awo ali apowo, agwidwa ndi mantha aakulu, pakuti Mulungu ali mʼgulu la olungama.
Yea, then shall they be in great fear; For Jehovah is with the race of the righteous.
6 Inu ochita zoyipa mumalepheretsa chikonzero cha anthu osauka, koma Yehova ndiye pothawirapo pawo.
Ye would put to shame the counsel of the poor; But Jehovah is their refuge.
7 Ndithu, chipulumutso cha Israeli chidzachokera ku Ziyoni! Pamene Yehova abwezeretsa ufulu wa anthu ake, Yakobo akondwere ndipo Israeli asangalale!
Oh that salvation for Israel would come out of Zion! When Jehovah bringeth back the captives of his people, Then shall Jacob rejoice, and Israel be glad.

< Masalimo 14 >