< Masalimo 14 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Chitsiru chimati mu mtima mwake, “Kulibe Mulungu.” Oterewa ndi oyipa ndipo ntchito zawo ndi zonyansa; palibe amene amachita zabwino.
Kathutkung: Devit Tamipathu ni a lungthung hoi, Cathut awmhoeh ati. A rawk toe. Panuet ka tho e hno doeh a sak. Hawinae ka sak e awm hoeh toe.
2 Yehova kumwamba wayangʼana pansi, kuyangʼana anthu onse kuti aone ngati alipo wina wanzeru, amene amafunafuna Mulungu.
Cathut ka tawng niteh, ka panuek thai e ao han na ou tie panue han ngai dawk, BAWIPA ni kalvan hoi tami capanaw hah a khet cathuk.
3 Onse atembenukira kumbali, onse pamodzi asanduka oyipa; palibe amene amachita zabwino, palibiretu ndi mmodzi yemwe.
Abuemlahoi lam a phen awh teh, cungtalah koung a rawk awh toe. Hawinae kasakkung apihai awmhoeh. Buet touh boehai awmhoeh.
4 Kodi anthu ochita zoyipawa sadziwa chilichonse? Akudya anthu anga ngati chakudya chawo ndipo satamanda Yehova?
Payonnae kasaknaw ni panuenae tawn awh hoeh ma aw. Rawca ca e patetlah ka taminaw hah a ca awh teh, BAWIPA kaw awh hoeh.
5 Awo ali apowo, agwidwa ndi mantha aakulu, pakuti Mulungu ali mʼgulu la olungama.
Hawvah, takinae kalen koe ao awh. Bangkongtetpawiteh, Cathut teh tami kalannaw koelah ao.
6 Inu ochita zoyipa mumalepheretsa chikonzero cha anthu osauka, koma Yehova ndiye pothawirapo pawo.
Tami karoedengnaw e pouknae teh a kaya sak awh. Hatei, BAWIPA teh ahnimae kânguenae doeh.
7 Ndithu, chipulumutso cha Israeli chidzachokera ku Ziyoni! Pamene Yehova abwezeretsa ufulu wa anthu ake, Yakobo akondwere ndipo Israeli asangalale!
Oe Isarel rungngangnae teh Zion hoi tâcawt naseh. BAWIPA ni san lah kaawm e taminaw a bankhai toteh, Jakop teh konawm naseh. Isarel hai lunghawi naseh.