< Masalimo 139 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Inu Yehova, mwandisanthula ndipo mukundidziwa.
Dāvida dziesma, dziedātāju vadonim. Kungs, Tu mani pārmani un pazīsti.
2 Inu mumadziwa pamene ndikhala pansi ndi pamene ndidzuka; mumazindikira maganizo anga muli kutali.
Tu zini manu sēdēšanu un celšanos, Tu noproti manas domas no tālienes.
3 Mumapenyetsetsa pamene ndikutuluka ndi kugona kwanga; mumadziwa njira zanga zonse.
Lai eju, lai guļu, Tu esi ap mani, un Tev zināmi visi mani ceļi.
4 Mawu asanatuluke pa lilime langa mumawadziwa bwinobwino, Inu Yehova.
Jo nav ne vārda uz manas mēles; redzi, Kungs, to visu Tu zini.
5 Mumandizinga kumbuyo ndi kutsogolo komwe; mwasanjika dzanja lanu pa ine.
Tu meties ap mani pakaļā un priekšā un turi Savu roku pār mani.
6 Nzeru zimenezi ndi zopitirira nzeru zanga, ndi zapamwamba kuti ine ndizipeze.
Šī atzīšana man ir visai brīnišķa un augsta, es to nevaru izprast.
7 Kodi ndingapite kuti kufuna kuzemba Mzimu wanu? Kodi ndingathawire kuti kuchoka pamaso panu?
Kur man būs aiziet no Tava Gara, un kur man būs bēgt no Tava vaiga?
8 Ndikakwera kumwamba, Inu muli komweko; ndikakagona ku malo a anthu akufa, Inu muli komweko. (Sheol h7585)
Ja es kāptu debesīs, tad Tu tur esi; ja es nogultos ellē, redzi, Tu tur arīdzan esi. (Sheol h7585)
9 Ngati ndiwulukira kotulukira dzuwa, ngati ndikakhala ku malekezero a nyanja,
Ja es ņemtu ausekļa spārnus un paliktu jūras galā.
10 kumenekonso dzanja lanu lidzanditsogolera, dzanja lanu lamanja lidzandigwiriziza.
Tad arī tur Tava roka mani vadīs, un Tava labā roka mani turēs.
11 Ndikanena kuti, “Zoonadi, mdima udzandibisa ndithu ndipo kuwunika kukhale mdima mondizungulira,”
Ja es sacītu: Lai tumsība mani apklāj un par nakti lai paliek gaisma ap mani:
12 komabe mdimawo sudzakhala mdima kwa Inu; usiku udzawala ngati masana, pakuti mdima uli ngati kuwunika kwa Inu.
Tad ir tumsība Tavā priekšā nebūtu tumša, un nakts spīdētu kā diena, tumsība būtu kā gaisma.
13 Pakuti Inu munalenga za mʼkati mwanga; munandiwumba pamodzi mʼmimba mwa amayi anga.
Jo Tu esi radījis manas īkstis, Tu mani esi apsedzis manas mātes miesās.
14 Ndimakuyamikani chifukwa ndinapangidwa mochititsa mantha ndi modabwitsa; ntchito zanu ndi zodabwitsa, zimenezi ndimazidziwa bwino lomwe.
Es Tev pateicos, ka es ļoti brīnišķi esmu darīts, brīnišķi ir Tavi darbi, un mana dvēsele to it labi zin.
15 Mapangidwe anga sanabisike pamaso panu pamene ndimapangidwa mʼmalo achinsinsi, pamene ndinkawumbidwa mwaluso mʼmimba ya amayi anga.
Mani kauli Tev nebija apslēpti, kad es slepenībā tapu darīts, kad es tapu iztaisīts zemes dziļumos.
16 Maso anu anaona thupi langa lisanawumbidwe. Masiku onse amene anapatsidwa kwa ine, analembedwa mʼbuku lanu asanayambe nʼkuwerengedwa komwe.
Tavas acis redzēja mani, vēl neiztaisītu pīti(miesas iedīgli), un visas nākamās dienas bija rakstītas Tavā grāmatā, kad vēl nebija nevienas.
17 Zolingalira zanu pa ine ndi zamtengowapatali, Inu Mulungu, ndi zosawerengeka ndithu!
Cik dārgas man ir Tavas domas, ak Dievs! Cik liels ir viņu skaits!
18 Ndikanaziwerenga, zikanakhala zochuluka kuposa mchenga; pamene ndadzuka, ndili nanube.
Kad tās jāskaita, tad viņu vairāk nekā smiltis. Es uzmostos un vēl esmu pie Tevis.
19 Ndi bwino mukanangopha anthu oyipa, Inu Mulungu! Chokereni inu anthu owononga anzanu!
Ak Dievs, kaut Tu bezdievīgo nokautu, un kaut asinsvainīgie no manis atstātos.
20 Amayankhula za Inu ndi zolinga zoyipa; adani anu amagwiritsa ntchito dzina lanu molakwika.
Tie par Tevi runā ar negantību un Tavi ienaidnieki lepojās ar viltu.
21 Kodi ine sindidana nawo amene amakudani, Inu Yehova? Kodi sindinyansidwa nawo amene amakuwukirani?
Vai man nebūs ienīdēt, kas Tevi, Kungs, ienīst, un ieriebt, kas pret Tevi ceļas?
22 Ndimadana nawo kwathunthu; ndi adani anga.
Ienīdēt es tos ienīstu, tie man ir ienaidnieki.
23 Santhuleni, Inu Mulungu ndipo mudziwe mtima wanga; Yeseni ndipo mudziwe zolingalira zanga.
Pārbaudi mani, ak Dievs, un atzīsti manu sirdi, izmeklē mani un atzīsti manas domas,
24 Onani ngati muli mayendedwe aliwonse oyipa mwa ine, ndipo munditsogolere mʼnjira yanu yamuyaya.
Un redzi, vai es esmu negantā ceļā, un vadi mani uz mūžīgu ceļu.

< Masalimo 139 >