< Masalimo 139 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Inu Yehova, mwandisanthula ndipo mukundidziwa.
[Psalm lal David] LEUM GOD, kom liyeyu ac eteyu.
2 Inu mumadziwa pamene ndikhala pansi ndi pamene ndidzuka; mumazindikira maganizo anga muli kutali.
Kom etu ma nukewa nga oru; Kom ne muta loes likiyu, kom etu nunak luk nukewa.
3 Mumapenyetsetsa pamene ndikutuluka ndi kugona kwanga; mumadziwa njira zanga zonse.
Kom liyeyu lah nga orekma, ku nga mongla; Kom etu mukuikui luk nukewa.
4 Mawu asanatuluke pa lilime langa mumawadziwa bwinobwino, Inu Yehova.
Meet liki na nga kaskas, Kom etu tari lah mea nga ac fahk.
5 Mumandizinga kumbuyo ndi kutsogolo komwe; mwasanjika dzanja lanu pa ine.
Kom apinyula ke siska nukewa, Kom karinginyu ke ku lom.
6 Nzeru zimenezi ndi zopitirira nzeru zanga, ndi zapamwamba kuti ine ndizipeze.
Etu lom keik uh arulana yohk, Yohk liki ma nga ku in kalem kac.
7 Kodi ndingapite kuti kufuna kuzemba Mzimu wanu? Kodi ndingathawire kuti kuchoka pamaso panu?
Nga ac som nu ya in kaingla liki kom? Nga ac kaing nu ya liki ye motom?
8 Ndikakwera kumwamba, Inu muli komweko; ndikakagona ku malo a anthu akufa, Inu muli komweko. (Sheol )
Nga fin som nu inkusrao, kom oasr we; Nga fin ona infulan misa, kom oasr pac we. (Sheol )
9 Ngati ndiwulukira kotulukira dzuwa, ngati ndikakhala ku malekezero a nyanja,
Nga finne sokla loesla liki kutulap, Ku muta yen loeslana nu roto,
10 kumenekonso dzanja lanu lidzanditsogolera, dzanja lanu lamanja lidzandigwiriziza.
Kom ac oasr pac we in pwenyu, Kom ac oasr pa ingo in kasreyu.
11 Ndikanena kuti, “Zoonadi, mdima udzandibisa ndithu ndipo kuwunika kukhale mdima mondizungulira,”
Nga ku in siyuk lohsr uh in wikinyula Ku kalem su rauniyula in ekla nu ke fong,
12 komabe mdimawo sudzakhala mdima kwa Inu; usiku udzawala ngati masana, pakuti mdima uli ngati kuwunika kwa Inu.
Tusruktu, lohsr uh el tia lohsr nu sum, Ac fong uh arulana kalem nu sum, oana len. Lohsr ac kalem oana sie nu sum.
13 Pakuti Inu munalenga za mʼkati mwanga; munandiwumba pamodzi mʼmimba mwa amayi anga.
Kom lumahla ip nukewa ke monuk; Kom oakiyuwi insien nina kiuk.
14 Ndimakuyamikani chifukwa ndinapangidwa mochititsa mantha ndi modabwitsa; ntchito zanu ndi zodabwitsa, zimenezi ndimazidziwa bwino lomwe.
Nga kaksakin kom mweyen fal mwet uh in sangeng sum. Ma nukewa kom oru, usrnguk ac wolana, Nga etu ouinge ke insiuk nufon.
15 Mapangidwe anga sanabisike pamaso panu pamene ndimapangidwa mʼmalo achinsinsi, pamene ndinkawumbidwa mwaluso mʼmimba ya amayi anga.
Ke mutawauk in lumweyuk sri keik uh, Ac oakiyuki wo insien nina kiuk, Ke nga kapkapak ingo in lukma, Kom nuna etu lah nga oasr we.
16 Maso anu anaona thupi langa lisanawumbidwe. Masiku onse amene anapatsidwa kwa ine, analembedwa mʼbuku lanu asanayambe nʼkuwerengedwa komwe.
Kom tuh liyeyu meet liki nga isusla. Pisen len ma oakiyuki nu sik tuh nga in moul Simla tari in book nutum Meet liki na kais sie ma inge mutawauk.
17 Zolingalira zanu pa ine ndi zamtengowapatali, Inu Mulungu, ndi zosawerengeka ndithu!
O God, arulana pus nunak lom, Ac arulana upa nu sik in kalem kac.
18 Ndikanaziwerenga, zikanakhala zochuluka kuposa mchenga; pamene ndadzuka, ndili nanube.
Nga fin oek, pisalos ac pus liki puk uh. Ke nga ngutalik, nga srakna muta yurum.
19 Ndi bwino mukanangopha anthu oyipa, Inu Mulungu! Chokereni inu anthu owononga anzanu!
O God, nga kena tuh kom in uniya mwet koluk! Nga arulana kena tuh mwet sulallal in fahsr likiyu.
20 Amayankhula za Inu ndi zolinga zoyipa; adani anu amagwiritsa ntchito dzina lanu molakwika.
Elos fahk ma koluk keim; Elos fahk kas na koluk lain Inem.
21 Kodi ine sindidana nawo amene amakudani, Inu Yehova? Kodi sindinyansidwa nawo amene amakuwukirani?
O LEUM GOD, nga arulana srungalos su srungakom! Nga kwaselos su tuyak lain Kom.
22 Ndimadana nawo kwathunthu; ndi adani anga.
Nga srungalos na pwaye; Nga oakalos mwet lokoalok luk.
23 Santhuleni, Inu Mulungu ndipo mudziwe mtima wanga; Yeseni ndipo mudziwe zolingalira zanga.
Liyeyu, O God, ac etu insiuk; Srikeyu, ac konauk nunak luk.
24 Onani ngati muli mayendedwe aliwonse oyipa mwa ine, ndipo munditsogolere mʼnjira yanu yamuyaya.
Suk lah oasr kutena ma sufal in nga Ac kolyu ke inkanek kawil nu tok.