< Masalimo 139 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Inu Yehova, mwandisanthula ndipo mukundidziwa.
למנצח לדוד מזמור יהוה חקרתני ותדע׃
2 Inu mumadziwa pamene ndikhala pansi ndi pamene ndidzuka; mumazindikira maganizo anga muli kutali.
אתה ידעת שבתי וקומי בנתה לרעי מרחוק׃
3 Mumapenyetsetsa pamene ndikutuluka ndi kugona kwanga; mumadziwa njira zanga zonse.
ארחי ורבעי זרית וכל דרכי הסכנתה׃
4 Mawu asanatuluke pa lilime langa mumawadziwa bwinobwino, Inu Yehova.
כי אין מלה בלשוני הן יהוה ידעת כלה׃
5 Mumandizinga kumbuyo ndi kutsogolo komwe; mwasanjika dzanja lanu pa ine.
אחור וקדם צרתני ותשת עלי כפכה׃
6 Nzeru zimenezi ndi zopitirira nzeru zanga, ndi zapamwamba kuti ine ndizipeze.
פלאיה דעת ממני נשגבה לא אוכל לה׃
7 Kodi ndingapite kuti kufuna kuzemba Mzimu wanu? Kodi ndingathawire kuti kuchoka pamaso panu?
אנה אלך מרוחך ואנה מפניך אברח׃
8 Ndikakwera kumwamba, Inu muli komweko; ndikakagona ku malo a anthu akufa, Inu muli komweko. (Sheol h7585)
אם אסק שמים שם אתה ואציעה שאול הנך׃ (Sheol h7585)
9 Ngati ndiwulukira kotulukira dzuwa, ngati ndikakhala ku malekezero a nyanja,
אשא כנפי שחר אשכנה באחרית ים׃
10 kumenekonso dzanja lanu lidzanditsogolera, dzanja lanu lamanja lidzandigwiriziza.
גם שם ידך תנחני ותאחזני ימינך׃
11 Ndikanena kuti, “Zoonadi, mdima udzandibisa ndithu ndipo kuwunika kukhale mdima mondizungulira,”
ואמר אך חשך ישופני ולילה אור בעדני׃
12 komabe mdimawo sudzakhala mdima kwa Inu; usiku udzawala ngati masana, pakuti mdima uli ngati kuwunika kwa Inu.
גם חשך לא יחשיך ממך ולילה כיום יאיר כחשיכה כאורה׃
13 Pakuti Inu munalenga za mʼkati mwanga; munandiwumba pamodzi mʼmimba mwa amayi anga.
כי אתה קנית כליתי תסכני בבטן אמי׃
14 Ndimakuyamikani chifukwa ndinapangidwa mochititsa mantha ndi modabwitsa; ntchito zanu ndi zodabwitsa, zimenezi ndimazidziwa bwino lomwe.
אודך על כי נוראות נפליתי נפלאים מעשיך ונפשי ידעת מאד׃
15 Mapangidwe anga sanabisike pamaso panu pamene ndimapangidwa mʼmalo achinsinsi, pamene ndinkawumbidwa mwaluso mʼmimba ya amayi anga.
לא נכחד עצמי ממך אשר עשיתי בסתר רקמתי בתחתיות ארץ׃
16 Maso anu anaona thupi langa lisanawumbidwe. Masiku onse amene anapatsidwa kwa ine, analembedwa mʼbuku lanu asanayambe nʼkuwerengedwa komwe.
גלמי ראו עיניך ועל ספרך כלם יכתבו ימים יצרו ולא אחד בהם׃
17 Zolingalira zanu pa ine ndi zamtengowapatali, Inu Mulungu, ndi zosawerengeka ndithu!
ולי מה יקרו רעיך אל מה עצמו ראשיהם׃
18 Ndikanaziwerenga, zikanakhala zochuluka kuposa mchenga; pamene ndadzuka, ndili nanube.
אספרם מחול ירבון הקיצתי ועודי עמך׃
19 Ndi bwino mukanangopha anthu oyipa, Inu Mulungu! Chokereni inu anthu owononga anzanu!
אם תקטל אלוה רשע ואנשי דמים סורו מני׃
20 Amayankhula za Inu ndi zolinga zoyipa; adani anu amagwiritsa ntchito dzina lanu molakwika.
אשר יאמרך למזמה נשא לשוא עריך׃
21 Kodi ine sindidana nawo amene amakudani, Inu Yehova? Kodi sindinyansidwa nawo amene amakuwukirani?
הלוא משנאיך יהוה אשנא ובתקוממיך אתקוטט׃
22 Ndimadana nawo kwathunthu; ndi adani anga.
תכלית שנאה שנאתים לאויבים היו לי׃
23 Santhuleni, Inu Mulungu ndipo mudziwe mtima wanga; Yeseni ndipo mudziwe zolingalira zanga.
חקרני אל ודע לבבי בחנני ודע שרעפי׃
24 Onani ngati muli mayendedwe aliwonse oyipa mwa ine, ndipo munditsogolere mʼnjira yanu yamuyaya.
וראה אם דרך עצב בי ונחני בדרך עולם׃

< Masalimo 139 >