< Masalimo 139 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Inu Yehova, mwandisanthula ndipo mukundidziwa.
Au maître chantre. Cantique de David. Éternel, tu me pénètres et me connais.
2 Inu mumadziwa pamene ndikhala pansi ndi pamene ndidzuka; mumazindikira maganizo anga muli kutali.
Tu sais quand je m'assieds et quand je me lève, de loin tu découvres ma pensée.
3 Mumapenyetsetsa pamene ndikutuluka ndi kugona kwanga; mumadziwa njira zanga zonse.
Tu me vois marcher et me reposer, et tu as connaissance de toutes mes voies.
4 Mawu asanatuluke pa lilime langa mumawadziwa bwinobwino, Inu Yehova.
Car la parole n'est pas encore sur ma langue, que déjà, Éternel, tu la connais tout entière.
5 Mumandizinga kumbuyo ndi kutsogolo komwe; mwasanjika dzanja lanu pa ine.
Tu m'enserres par devant et par derrière, et tu tiens ta main sur moi.
6 Nzeru zimenezi ndi zopitirira nzeru zanga, ndi zapamwamba kuti ine ndizipeze.
Cette science est une merveille pour moi; elle est trop élevée, je ne puis la saisir.
7 Kodi ndingapite kuti kufuna kuzemba Mzimu wanu? Kodi ndingathawire kuti kuchoka pamaso panu?
Où irai-je loin de ton Esprit, et où fuirai-je loin de ta face?
8 Ndikakwera kumwamba, Inu muli komweko; ndikakagona ku malo a anthu akufa, Inu muli komweko. (Sheol )
Si je monte aux Cieux, tu y es; si je prends les Enfers pour ma couche, tu es là! (Sheol )
9 Ngati ndiwulukira kotulukira dzuwa, ngati ndikakhala ku malekezero a nyanja,
Si, me soulevant sur les ailes de l'aurore, j'allais me loger au bout de la mer,
10 kumenekonso dzanja lanu lidzanditsogolera, dzanja lanu lamanja lidzandigwiriziza.
là aussi ta main me conduirait, et ta droite me saisirait.
11 Ndikanena kuti, “Zoonadi, mdima udzandibisa ndithu ndipo kuwunika kukhale mdima mondizungulira,”
Et si je dis: Qu'autour de moi il n'y ait que ténèbres et que la clarté qui m'entoure se change en nuit!
12 komabe mdimawo sudzakhala mdima kwa Inu; usiku udzawala ngati masana, pakuti mdima uli ngati kuwunika kwa Inu.
les ténèbres mêmes ne seront pas sombres pour toi, et la nuit sera claire comme le jour, les ténèbres seront ce qu'est la lumière.
13 Pakuti Inu munalenga za mʼkati mwanga; munandiwumba pamodzi mʼmimba mwa amayi anga.
C'est toi en effet qui as formé mes reins, m'as tissé dans le sein maternel.
14 Ndimakuyamikani chifukwa ndinapangidwa mochititsa mantha ndi modabwitsa; ntchito zanu ndi zodabwitsa, zimenezi ndimazidziwa bwino lomwe.
je te loue de la merveille de ma structure. Tes œuvres sont merveilleuses, et mon âme le reconnaît profondément.
15 Mapangidwe anga sanabisike pamaso panu pamene ndimapangidwa mʼmalo achinsinsi, pamene ndinkawumbidwa mwaluso mʼmimba ya amayi anga.
Mon corps n'était point caché à tes yeux, quand j'étais formé mystérieusement dans les entrailles de la terre, comme des fils qui s'entrelacent.
16 Maso anu anaona thupi langa lisanawumbidwe. Masiku onse amene anapatsidwa kwa ine, analembedwa mʼbuku lanu asanayambe nʼkuwerengedwa komwe.
Quand je n'étais qu'une matière informe, tes yeux me voyaient; et dans ton livre étaient marqués tous ensemble mes jours déjà déterminés, lorsque aucun d'eux n'existait.
17 Zolingalira zanu pa ine ndi zamtengowapatali, Inu Mulungu, ndi zosawerengeka ndithu!
Que tes pensées, ô Dieu, sont incompréhensibles pour moi! que la somme en est immense!
18 Ndikanaziwerenga, zikanakhala zochuluka kuposa mchenga; pamene ndadzuka, ndili nanube.
Veux-je les compter, les grains de sable sont moins nombreux; je m'éveille, et je suis encore avec toi.
19 Ndi bwino mukanangopha anthu oyipa, Inu Mulungu! Chokereni inu anthu owononga anzanu!
O Dieu, puisses-tu faire mourir l'impie! Hommes de sang, éloignez-vous de moi!
20 Amayankhula za Inu ndi zolinga zoyipa; adani anu amagwiritsa ntchito dzina lanu molakwika.
Eux, qui parlent de toi en commettant le crime, disent ton nom pour mentir, ce sont tes ennemis.
21 Kodi ine sindidana nawo amene amakudani, Inu Yehova? Kodi sindinyansidwa nawo amene amakuwukirani?
Ne haïrais-je pas, Éternel, ceux qui te haïssent, et n'aurais-je pas de l'horreur pour tes adversaires?
22 Ndimadana nawo kwathunthu; ndi adani anga.
Je les hais d'une haine sans réserve; ils sont des ennemis pour moi!
23 Santhuleni, Inu Mulungu ndipo mudziwe mtima wanga; Yeseni ndipo mudziwe zolingalira zanga.
Sonde-moi, ô Dieu, et pénètre mon cœur; éprouve-moi, et connais mes pensées!
24 Onani ngati muli mayendedwe aliwonse oyipa mwa ine, ndipo munditsogolere mʼnjira yanu yamuyaya.
Et vois si le chemin que je suis, est celui du crime, et conduis-moi sur la voie des anciens temps!