< Masalimo 139 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Inu Yehova, mwandisanthula ndipo mukundidziwa.
To the chief Musician, A Psalm of David. O LORD, thou hast searched me, and known [me].
2 Inu mumadziwa pamene ndikhala pansi ndi pamene ndidzuka; mumazindikira maganizo anga muli kutali.
Thou knowest my down-sitting and my up rising, thou understandest my thought afar off.
3 Mumapenyetsetsa pamene ndikutuluka ndi kugona kwanga; mumadziwa njira zanga zonse.
Thou compassest my path and my lying down, and art acquainted [with] all my ways.
4 Mawu asanatuluke pa lilime langa mumawadziwa bwinobwino, Inu Yehova.
For [there is] not a word on my tongue, [but] lo, O LORD, thou knowest it altogether.
5 Mumandizinga kumbuyo ndi kutsogolo komwe; mwasanjika dzanja lanu pa ine.
Thou hast beset me behind and before, and laid thy hand upon me.
6 Nzeru zimenezi ndi zopitirira nzeru zanga, ndi zapamwamba kuti ine ndizipeze.
[Such] knowledge [is] too wonderful for me; it is high, I cannot [attain] to it.
7 Kodi ndingapite kuti kufuna kuzemba Mzimu wanu? Kodi ndingathawire kuti kuchoka pamaso panu?
Whither shall I go from thy spirit? or whither shall I flee from thy presence?
8 Ndikakwera kumwamba, Inu muli komweko; ndikakagona ku malo a anthu akufa, Inu muli komweko. (Sheol h7585)
If I ascend into heaven, thou [art] there: if I make my bed in hell, behold, thou [art there]. (Sheol h7585)
9 Ngati ndiwulukira kotulukira dzuwa, ngati ndikakhala ku malekezero a nyanja,
[If] I take the wings of the morning, [and] dwell in the uttermost parts of the sea;
10 kumenekonso dzanja lanu lidzanditsogolera, dzanja lanu lamanja lidzandigwiriziza.
Even there shall thy hand lead me, and thy right hand shall hold me.
11 Ndikanena kuti, “Zoonadi, mdima udzandibisa ndithu ndipo kuwunika kukhale mdima mondizungulira,”
If I say, Surely the darkness shall cover me; even the night shall be light about me.
12 komabe mdimawo sudzakhala mdima kwa Inu; usiku udzawala ngati masana, pakuti mdima uli ngati kuwunika kwa Inu.
Yes, the darkness hideth not from thee; but the night shineth as the day: the darkness and the light [are] both alike [to thee].
13 Pakuti Inu munalenga za mʼkati mwanga; munandiwumba pamodzi mʼmimba mwa amayi anga.
For thou hast possessed my reins: thou hast covered me in my mother's womb.
14 Ndimakuyamikani chifukwa ndinapangidwa mochititsa mantha ndi modabwitsa; ntchito zanu ndi zodabwitsa, zimenezi ndimazidziwa bwino lomwe.
I will praise thee: for I am fearfully [and] wonderfully made: wonderful [are] thy works; and [that] my soul well knoweth.
15 Mapangidwe anga sanabisike pamaso panu pamene ndimapangidwa mʼmalo achinsinsi, pamene ndinkawumbidwa mwaluso mʼmimba ya amayi anga.
My substance was not hid from thee when I was made in secret, [and] curiously formed in the lowest parts of the earth.
16 Maso anu anaona thupi langa lisanawumbidwe. Masiku onse amene anapatsidwa kwa ine, analembedwa mʼbuku lanu asanayambe nʼkuwerengedwa komwe.
Thy eyes saw my substance, yet being imperfect; and in thy book all [my members] were written, [which] in continuance were fashioned, when [as yet there was] none of them.
17 Zolingalira zanu pa ine ndi zamtengowapatali, Inu Mulungu, ndi zosawerengeka ndithu!
How precious also are thy thoughts to me, O God! how great is the sum of them!
18 Ndikanaziwerenga, zikanakhala zochuluka kuposa mchenga; pamene ndadzuka, ndili nanube.
[If] I should count them, they are more in number than the sand: when I awake, I am still with thee.
19 Ndi bwino mukanangopha anthu oyipa, Inu Mulungu! Chokereni inu anthu owononga anzanu!
Surely thou wilt slay the wicked, O God: depart from me therefore, ye bloody men.
20 Amayankhula za Inu ndi zolinga zoyipa; adani anu amagwiritsa ntchito dzina lanu molakwika.
For they speak against thee wickedly, [and] thy enemies take [thy name] in vain.
21 Kodi ine sindidana nawo amene amakudani, Inu Yehova? Kodi sindinyansidwa nawo amene amakuwukirani?
Do not I hate them, O LORD, that hate thee? and am not I grieved with those that rise up against thee?
22 Ndimadana nawo kwathunthu; ndi adani anga.
I hate them with perfect hatred: I count them my enemies.
23 Santhuleni, Inu Mulungu ndipo mudziwe mtima wanga; Yeseni ndipo mudziwe zolingalira zanga.
Search me, O God, and know my heart; try me, and know my thoughts:
24 Onani ngati muli mayendedwe aliwonse oyipa mwa ine, ndipo munditsogolere mʼnjira yanu yamuyaya.
And see if [there is any] wicked way in me, and lead me in the way everlasting.

< Masalimo 139 >