< Masalimo 139 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Inu Yehova, mwandisanthula ndipo mukundidziwa.
Yahweh, you have examined me, and you know [everything about] me.
2 Inu mumadziwa pamene ndikhala pansi ndi pamene ndidzuka; mumazindikira maganizo anga muli kutali.
You know when I sit down and when I stand up. [Even though you are] far away from me, you know what I am thinking.
3 Mumapenyetsetsa pamene ndikutuluka ndi kugona kwanga; mumadziwa njira zanga zonse.
When I travel and when I lie down, you know everything that I do.
4 Mawu asanatuluke pa lilime langa mumawadziwa bwinobwino, Inu Yehova.
Yahweh, even before I say [MTY] anything, you know everything that I am going to say!
5 Mumandizinga kumbuyo ndi kutsogolo komwe; mwasanjika dzanja lanu pa ine.
You protect me on all sides; you put your hand on me [to protect me with your power] [MTY].
6 Nzeru zimenezi ndi zopitirira nzeru zanga, ndi zapamwamba kuti ine ndizipeze.
I am not able to understand that you know [everything about me]. That is too great for me to really understand.
7 Kodi ndingapite kuti kufuna kuzemba Mzimu wanu? Kodi ndingathawire kuti kuchoka pamaso panu?
(Where could I go to escape from your Spirit?/I could not go anywhere to escape from your Spirit.) [RHQ] (Where could I go to get away from you?/I could not go anywhere to get away from you.) [RHQ]
8 Ndikakwera kumwamba, Inu muli komweko; ndikakagona ku malo a anthu akufa, Inu muli komweko. (Sheol h7585)
If I went up to heaven, you would be there. If I lay down in the place where the dead people are, you would be there. (Sheol h7585)
9 Ngati ndiwulukira kotulukira dzuwa, ngati ndikakhala ku malekezero a nyanja,
If I had wings and flew very far east [MTY], or if I flew west and made a place to live [on an island] in the ocean,
10 kumenekonso dzanja lanu lidzanditsogolera, dzanja lanu lamanja lidzandigwiriziza.
you would be there also, to lead me by your hand, and you would help me.
11 Ndikanena kuti, “Zoonadi, mdima udzandibisa ndithu ndipo kuwunika kukhale mdima mondizungulira,”
I could request the darkness to hide me, or I could request the light around me to become darkness,
12 komabe mdimawo sudzakhala mdima kwa Inu; usiku udzawala ngati masana, pakuti mdima uli ngati kuwunika kwa Inu.
but even [if that happened], the darkness would not be darkness for you! For you, the night is [as bright] as the daytime is, because for you, daylight and darkness are (not different/the same).
13 Pakuti Inu munalenga za mʼkati mwanga; munandiwumba pamodzi mʼmimba mwa amayi anga.
You created [all] the parts of my body; you put [the parts of] my body together when I was still in my mother’s womb.
14 Ndimakuyamikani chifukwa ndinapangidwa mochititsa mantha ndi modabwitsa; ntchito zanu ndi zodabwitsa, zimenezi ndimazidziwa bwino lomwe.
I praise you because you made my [body in a very] awesome and wonderful way. Everything that you do is amazing! I know that very well.
15 Mapangidwe anga sanabisike pamaso panu pamene ndimapangidwa mʼmalo achinsinsi, pamene ndinkawumbidwa mwaluso mʼmimba ya amayi anga.
When my body was being formed, while it was being put together where no one else could see it, you saw it!
16 Maso anu anaona thupi langa lisanawumbidwe. Masiku onse amene anapatsidwa kwa ine, analembedwa mʼbuku lanu asanayambe nʼkuwerengedwa komwe.
You saw me before I was born. You wrote in your book the number of days that you had decided that I would live. You did that before any of those days had [even] started!
17 Zolingalira zanu pa ine ndi zamtengowapatali, Inu Mulungu, ndi zosawerengeka ndithu!
God, what you think about me is very precious (OR, is very hard to understand). There is a great number of things that you think about.
18 Ndikanaziwerenga, zikanakhala zochuluka kuposa mchenga; pamene ndadzuka, ndili nanube.
If I could count them, [I would see that] they are more than the grains of sand [at the seashore]. And when I wake up, I am still with you [and I know that there are still more of your thoughts about me to count].
19 Ndi bwino mukanangopha anthu oyipa, Inu Mulungu! Chokereni inu anthu owononga anzanu!
God, I desire that you would kill all the wicked people! And I wish that violent [MTY] men would (leave/go away from) me.
20 Amayankhula za Inu ndi zolinga zoyipa; adani anu amagwiritsa ntchito dzina lanu molakwika.
They say wicked/malicious things about you; they slander your name.
21 Kodi ine sindidana nawo amene amakudani, Inu Yehova? Kodi sindinyansidwa nawo amene amakuwukirani?
Yahweh, I certainly [RHQ] hate those who hate you! And I despise [RHQ] those who rebel against you.
22 Ndimadana nawo kwathunthu; ndi adani anga.
I hate them completely, and I consider that they are my enemies.
23 Santhuleni, Inu Mulungu ndipo mudziwe mtima wanga; Yeseni ndipo mudziwe zolingalira zanga.
God, search my inner being; find out what I am thinking!
24 Onani ngati muli mayendedwe aliwonse oyipa mwa ine, ndipo munditsogolere mʼnjira yanu yamuyaya.
Find out whether there is anything evil in my [inner being], and lead me along the road [that leads to my being with you] forever.

< Masalimo 139 >