< Masalimo 139 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Inu Yehova, mwandisanthula ndipo mukundidziwa.
Kuom jatend wer. Zaburi mar Daudi. Yaye Jehova Nyasaye, isenona kendo ingʼeya.
2 Inu mumadziwa pamene ndikhala pansi ndi pamene ndidzuka; mumazindikira maganizo anga muli kutali.
Ingʼeya sa ma abet piny nyaka sa ma aa malo; adier, ingʼeyo parona gi kuma bor.
3 Mumapenyetsetsa pamene ndikutuluka ndi kugona kwanga; mumadziwa njira zanga zonse.
Bende ingʼeyo yorega ma aluwo kod kuonde ma ayweyoe; yorena duto oyangoreni maber.
4 Mawu asanatuluke pa lilime langa mumawadziwa bwinobwino, Inu Yehova.
Kata kapok wach moro owuok e dhoga to ingʼeye malongʼo, yaye Jehova Nyasaye.
5 Mumandizinga kumbuyo ndi kutsogolo komwe; mwasanjika dzanja lanu pa ine.
Ilwora koni gi koni mi iketa diere; adier, iseuma duto gi lweti.
6 Nzeru zimenezi ndi zopitirira nzeru zanga, ndi zapamwamba kuti ine ndizipeze.
Rieko ma kamano lichna miwuoro, kendo otutna moyombo pacha.
7 Kodi ndingapite kuti kufuna kuzemba Mzimu wanu? Kodi ndingathawire kuti kuchoka pamaso panu?
Dadhi kure eka apond ne Roho mari? Koso kanye ma daring adhiye mondo apondni?
8 Ndikakwera kumwamba, Inu muli komweko; ndikakagona ku malo a anthu akufa, Inu muli komweko. (Sheol h7585)
Ka aidho e polo, to in kuno; ka aloso kitandana e bur matut, to in kuno. (Sheol h7585)
9 Ngati ndiwulukira kotulukira dzuwa, ngati ndikakhala ku malekezero a nyanja,
Ka aidho yamb kogwen mondo otera e tok nam komachielo,
10 kumenekonso dzanja lanu lidzanditsogolera, dzanja lanu lamanja lidzandigwiriziza.
to kata kuno bende lweti biro telonae, kendo lweti ma korachwich biro maka motegno.
11 Ndikanena kuti, “Zoonadi, mdima udzandibisa ndithu ndipo kuwunika kukhale mdima mondizungulira,”
Ka awacho niya, “Mudho biro ima adier kendo ler biro lokorena otieno,”
12 komabe mdimawo sudzakhala mdima kwa Inu; usiku udzawala ngati masana, pakuti mdima uli ngati kuwunika kwa Inu.
to in mudho ok timni mudho kendo otieno rienyni ka odiechiengʼ, nimar mudho chaloni ler.
13 Pakuti Inu munalenga za mʼkati mwanga; munandiwumba pamodzi mʼmimba mwa amayi anga.
In ema ne ichweyo dhanda maiye, adier, ne ingʼina maber gi ei minwa.
14 Ndimakuyamikani chifukwa ndinapangidwa mochititsa mantha ndi modabwitsa; ntchito zanu ndi zodabwitsa, zimenezi ndimazidziwa bwino lomwe.
Apaki nikech ne ichweya mongʼith kendo malich miwuoro; tijeni misetimo lich, kendo angʼeyo mano maber.
15 Mapangidwe anga sanabisike pamaso panu pamene ndimapangidwa mʼmalo achinsinsi, pamene ndinkawumbidwa mwaluso mʼmimba ya amayi anga.
Fuonde mag ringra ne ok opondoni, kane ochweya ei minwa, kane ochwe ringra e kama opondo,
16 Maso anu anaona thupi langa lisanawumbidwe. Masiku onse amene anapatsidwa kwa ine, analembedwa mʼbuku lanu asanayambe nʼkuwerengedwa komwe.
wangʼi ne oneno ringra ei minwa; ndalona duto e piny-ka ne ondiki chon gi lala, e kitabu mari kane pok kata achiel kuomgi obetie.
17 Zolingalira zanu pa ine ndi zamtengowapatali, Inu Mulungu, ndi zosawerengeka ndithu!
Mano kaka pachi tutna, yaye Nyasaye! Mano kaka gingʼeny mokalo akwana kargi duto!
18 Ndikanaziwerenga, zikanakhala zochuluka kuposa mchenga; pamene ndadzuka, ndili nanube.
Ka dine bed ni anyalo kwanogi, to dine giloyo kuoyo gi ngʼeny. Sa ma achiew to ayudo ni pod an mana kodi.
19 Ndi bwino mukanangopha anthu oyipa, Inu Mulungu! Chokereni inu anthu owononga anzanu!
Yaye Jehova Nyasaye, mad iyie ineg joma timbegi richo! Ayiuru buta, un joma rich chwero remb ji omakogi!
20 Amayankhula za Inu ndi zolinga zoyipa; adani anu amagwiritsa ntchito dzina lanu molakwika.
Giwuoyo kuomi gi paro marach; adier, wasiki tiyo gi nyingi e yo marach.
21 Kodi ine sindidana nawo amene amakudani, Inu Yehova? Kodi sindinyansidwa nawo amene amakuwukirani?
Donge amon gi jomamon kodi, yaye Jehova Nyasaye, koso donge ok awinjra gi joma chungʼ mondo oked kodi?
22 Ndimadana nawo kwathunthu; ndi adani anga.
Achayogi kendo aonge kodgi gi tich adier akwanogi kaka wasika.
23 Santhuleni, Inu Mulungu ndipo mudziwe mtima wanga; Yeseni ndipo mudziwe zolingalira zanga.
Nona, yaye Jehova Nyasaye, mondo ingʼe chunya; tema, mondo ingʼe pacha.
24 Onani ngati muli mayendedwe aliwonse oyipa mwa ine, ndipo munditsogolere mʼnjira yanu yamuyaya.
Tim kamano mondo ineane ka nitie gimoro marach kuoma, mondo itera e yor ngima mochwere.

< Masalimo 139 >