< Masalimo 139 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Inu Yehova, mwandisanthula ndipo mukundidziwa.
(Til Sangmesteren. Af David. En Salme.) HERRE, du ransager mig og kender mig!
2 Inu mumadziwa pamene ndikhala pansi ndi pamene ndidzuka; mumazindikira maganizo anga muli kutali.
Du ved, når jeg står op, du fatter min Tanke i Frastand,
3 Mumapenyetsetsa pamene ndikutuluka ndi kugona kwanga; mumadziwa njira zanga zonse.
du har Rede på, hvor jeg går eller ligger, og alle mine Veje kender du grant.
4 Mawu asanatuluke pa lilime langa mumawadziwa bwinobwino, Inu Yehova.
Thi før Ordet er til på min Tunge, se, da ved du det, HERRE, til fulde.
5 Mumandizinga kumbuyo ndi kutsogolo komwe; mwasanjika dzanja lanu pa ine.
Bagfra og forfra omslutter du mig, du lægger din Hånd på mig.
6 Nzeru zimenezi ndi zopitirira nzeru zanga, ndi zapamwamba kuti ine ndizipeze.
At fatte det er mig for underfuldt, for højt, jeg evner det ikke!
7 Kodi ndingapite kuti kufuna kuzemba Mzimu wanu? Kodi ndingathawire kuti kuchoka pamaso panu?
Hvorhen skal jeg gå for din Ånd, og hvor skal jeg fly for dit Åsyn?
8 Ndikakwera kumwamba, Inu muli komweko; ndikakagona ku malo a anthu akufa, Inu muli komweko. (Sheol h7585)
Farer jeg op til Himlen, da er du der, reder jeg Leje i Dødsriget, så er du der; (Sheol h7585)
9 Ngati ndiwulukira kotulukira dzuwa, ngati ndikakhala ku malekezero a nyanja,
tager jeg Morgenrødens Vinger, fæster jeg Bo, hvor Havet ender,
10 kumenekonso dzanja lanu lidzanditsogolera, dzanja lanu lamanja lidzandigwiriziza.
da vil din Hånd også lede mig der, din højre holde mig fast!
11 Ndikanena kuti, “Zoonadi, mdima udzandibisa ndithu ndipo kuwunika kukhale mdima mondizungulira,”
Og siger jeg: "Mørket skal skjule mig, Lyset blive Nat omkring mig!"
12 komabe mdimawo sudzakhala mdima kwa Inu; usiku udzawala ngati masana, pakuti mdima uli ngati kuwunika kwa Inu.
så er Mørket ej mørkt for dig, og Natten er klar som Dagen, Mørket er som Lyset.
13 Pakuti Inu munalenga za mʼkati mwanga; munandiwumba pamodzi mʼmimba mwa amayi anga.
Thi du har dannet mine Nyrer, vævet mig i Moders Liv.
14 Ndimakuyamikani chifukwa ndinapangidwa mochititsa mantha ndi modabwitsa; ntchito zanu ndi zodabwitsa, zimenezi ndimazidziwa bwino lomwe.
Jeg vil takke dig, fordi jeg er underfuldt skabt; underfulde er dine Gerninger, det kender min Sjæl til fulde.
15 Mapangidwe anga sanabisike pamaso panu pamene ndimapangidwa mʼmalo achinsinsi, pamene ndinkawumbidwa mwaluso mʼmimba ya amayi anga.
Mine Ben var ikke skjult for dig, da jeg blev skabt i Løndom, virket i Jordens Dyb;
16 Maso anu anaona thupi langa lisanawumbidwe. Masiku onse amene anapatsidwa kwa ine, analembedwa mʼbuku lanu asanayambe nʼkuwerengedwa komwe.
som Foster så dine Øjne mig, i din Bog var de alle skrevet, Dagene var bestemt, før en eneste af dem var kommet.
17 Zolingalira zanu pa ine ndi zamtengowapatali, Inu Mulungu, ndi zosawerengeka ndithu!
Hvor kostelige er dine Tanker mig, Gud, hvor stor er dog deres Sum!
18 Ndikanaziwerenga, zikanakhala zochuluka kuposa mchenga; pamene ndadzuka, ndili nanube.
Tæller jeg dem, er de flere end Sandet, jeg vågner - og end er jeg hos dig.
19 Ndi bwino mukanangopha anthu oyipa, Inu Mulungu! Chokereni inu anthu owononga anzanu!
Vilde du dog dræbe de gudløse, Gud, måtte Blodets Mænd vige fra mig,
20 Amayankhula za Inu ndi zolinga zoyipa; adani anu amagwiritsa ntchito dzina lanu molakwika.
de, som taler om dig på Skrømt og sværger falsk ved dit Navn.
21 Kodi ine sindidana nawo amene amakudani, Inu Yehova? Kodi sindinyansidwa nawo amene amakuwukirani?
Jeg hader jo dem, der hader dig, HERRE, og væmmes ved dem, der står dig imod;
22 Ndimadana nawo kwathunthu; ndi adani anga.
med fuldt Had bader jeg dem, de er også mine Fjender.
23 Santhuleni, Inu Mulungu ndipo mudziwe mtima wanga; Yeseni ndipo mudziwe zolingalira zanga.
Ransag mig, Gud, og kend mit Hjerte, prøv mig og kend mine Tanker!
24 Onani ngati muli mayendedwe aliwonse oyipa mwa ine, ndipo munditsogolere mʼnjira yanu yamuyaya.
Se, om jeg er på Smertens Vej, og led mig på Evigheds Vej!

< Masalimo 139 >