< Masalimo 139 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Inu Yehova, mwandisanthula ndipo mukundidziwa.
Kathutkung: Devit Oe BAWIPA, nang ni na pâphue teh na panue toe.
2 Inu mumadziwa pamene ndikhala pansi ndi pamene ndidzuka; mumazindikira maganizo anga muli kutali.
Kai ka tahungnae, ka thawnae pueng hah na panue. Kaie ka pouknae pueng hai ahlanae koehoi na panue.
3 Mumapenyetsetsa pamene ndikutuluka ndi kugona kwanga; mumadziwa njira zanga zonse.
Ka ceinae lamthung hai thoseh, ka inae hai thoseh, na pâphue teh, ka coungnae puenghai na panue.
4 Mawu asanatuluke pa lilime langa mumawadziwa bwinobwino, Inu Yehova.
Kai ni lawk kam touh boehai ka dei hoeh nakunghai Oe BAWIPA, nang ni koung na panue.
5 Mumandizinga kumbuyo ndi kutsogolo komwe; mwasanjika dzanja lanu pa ine.
Nang ni kai pet na kalup teh, kaie van vah na kut hah na toung toe.
6 Nzeru zimenezi ndi zopitirira nzeru zanga, ndi zapamwamba kuti ine ndizipeze.
Hot patet e panuenae teh kângairu, arasang, kai ni ka phat thai hoeh.
7 Kodi ndingapite kuti kufuna kuzemba Mzimu wanu? Kodi ndingathawire kuti kuchoka pamaso panu?
Nange Muitha hoi hlout nahanelah nâmouh ka cei thai han va. Na hmalah hoi ka hlout nahanelah nâmouh ka cei thai han va.
8 Ndikakwera kumwamba, Inu muli komweko; ndikakagona ku malo a anthu akufa, Inu muli komweko. (Sheol )
Kalvan ka luen pawiteh hawvah nang teh na o. Phuen koe yannae ka phai nakunghai hawvah nang teh na o. (Sheol )
9 Ngati ndiwulukira kotulukira dzuwa, ngati ndikakhala ku malekezero a nyanja,
Amom ratheinaw ka lat niteh, tuipui avanglae rai koe kaawm nakunghai,
10 kumenekonso dzanja lanu lidzanditsogolera, dzanja lanu lamanja lidzandigwiriziza.
hote hmuen koehai Bawipa e kut ni na thak teh, aranglae kut ni na kuet han.
11 Ndikanena kuti, “Zoonadi, mdima udzandibisa ndithu ndipo kuwunika kukhale mdima mondizungulira,”
Hmonae ni ka ramuk nakunghai, karum hai kaie tengpam vah angnae lah ao han.
12 komabe mdimawo sudzakhala mdima kwa Inu; usiku udzawala ngati masana, pakuti mdima uli ngati kuwunika kwa Inu.
Bawipa hmalah hmonae ni banghai ramuk thai mahoeh. Karum teh khodai patetlah a ang. Hmonae hoi angnae teh reikâvan.
13 Pakuti Inu munalenga za mʼkati mwanga; munandiwumba pamodzi mʼmimba mwa amayi anga.
Bawipa ni kaie kuen hah a sak teh, anu von thungvah kai hah na ramuk toe.
14 Ndimakuyamikani chifukwa ndinapangidwa mochititsa mantha ndi modabwitsa; ntchito zanu ndi zodabwitsa, zimenezi ndimazidziwa bwino lomwe.
Kai ni na pholen han. Bangkongtetpawiteh, takikatho lah, kângailah a ru. Ka hringnae ni kacaicalah a panue.
15 Mapangidwe anga sanabisike pamaso panu pamene ndimapangidwa mʼmalo achinsinsi, pamene ndinkawumbidwa mwaluso mʼmimba ya amayi anga.
Kai hah arulahoi na sak teh, talai thung vah na pahlawm navah, ka tak teh na hmalah hro lah awm hoeh.
16 Maso anu anaona thupi langa lisanawumbidwe. Masiku onse amene anapatsidwa kwa ine, analembedwa mʼbuku lanu asanayambe nʼkuwerengedwa komwe.
Nange mit niteh, kamnuek hoeh rae ka tak hai na hmu toe. Kai hanelah na hmoun e hninthanaw hnin touh boehai ao hoehnahlan hoiyah nama e cauk dawk ngit na thut e lah ao toe.
17 Zolingalira zanu pa ine ndi zamtengowapatali, Inu Mulungu, ndi zosawerengeka ndithu!
Oe Cathut, kai dawkvah nange pouknae teh aphu o poung. Banghloi apap tangngak.
18 Ndikanaziwerenga, zikanakhala zochuluka kuposa mchenga; pamene ndadzuka, ndili nanube.
Hote pouknae teh parei han pawiteh, sadi hlak hai apap han doeh. Ka kâhlaw toteh nang hoi pou ka o.
19 Ndi bwino mukanangopha anthu oyipa, Inu Mulungu! Chokereni inu anthu owononga anzanu!
Oe Cathut, tamikaponaw hah na thet pawiteh ahawi han doeh. Tami thei hanlah thi ka phuen e naw, kai koehoi tâcawt awh.
20 Amayankhula za Inu ndi zolinga zoyipa; adani anu amagwiritsa ntchito dzina lanu molakwika.
Ahnimouh teh, ponae lahoi Bawipa tarannae lawk a dei awh. Nange tarannaw ni na min hah ayawmyin lah a hno awh.
21 Kodi ine sindidana nawo amene amakudani, Inu Yehova? Kodi sindinyansidwa nawo amene amakuwukirani?
Oe BAWIPA, nang ni na hmuhma e naw hai kai ni hai ka hmuhma nahoehmaw. Nang ka tarannaw hai kai ni ka panuet nahoehmaw.
22 Ndimadana nawo kwathunthu; ndi adani anga.
Kai ni ahnimouh hah puenghoi ka hmuhma. Ka taran lah doeh ka pouk.
23 Santhuleni, Inu Mulungu ndipo mudziwe mtima wanga; Yeseni ndipo mudziwe zolingalira zanga.
Oe Cathut, kai hah na pâphue teh, kaie ka lungthin hah hmawt haw. Kai hah na noumcai nateh ka pouknae pueng panuek haw.
24 Onani ngati muli mayendedwe aliwonse oyipa mwa ine, ndipo munditsogolere mʼnjira yanu yamuyaya.
Kai ni lamthung kathout dawk ka dawn ou, ka dawn hoeh ou tie na khen nateh, a yungyoe e lamthung dawk na hrawi haw.