< Masalimo 138 >

1 Salimo la Davide. Ndidzakuyamikani Yehova ndi mtima wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zokutamandani pamaso pa “milungu.”
Agyamanak kenka iti amin a pusok; iti sangoanan dagiti dios agkantaak kadagiti pagdaydayaw kenka.
2 Ndidzagwada kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera ndipo ndidzayamika dzina lanu chifukwa cha chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu, pakuti Inu mwakuza dzina lanu ndi mawu anu kupambana zinthu zonse.
Agrukbabak iti nasantoan a templom ken pagyamanak ti naganmo gapu iti kinapudnom iti tulagmo ken iti kinamatalekmo. Intan-okmo ti saom ken ti naganmo iti isuamin.
3 Pamene ndinayitana, munandiyankha; munandisandutsa wamphamvu ndi wolimba mtima.
Iti aldaw nga immawagak kenka, sinungbatannak; pinaregtam ken pinapigsam ti kararruak.
4 Mafumu onse a dziko lapansi akuyamikeni Yehova, pamene amva mawu a pakamwa panu.
Agyamanto kenka dagiti amin nga ar-ari iti daga, O Yahweh, ta mangegda dagiti sasao manipud iti ngiwatmo.
5 Iwo ayimbe za njira za Yehova, pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukulu.
Pudno, ikantadanto ti maipapan kadagiti aramid ni Yahweh, ta naindaklan ti dayag ni Yahweh.
6 Ngakhale kuti Yehova ngokwezeka, amasamalira odzichepetsa, koma anthu onyada amawadziwira chapatali.
Ta uray no nangato ni Yahweh, kailalaanna latta dagiti nababa, ngem am-ammona dagiti napannakel uray no adayoda.
7 Ngakhale ndiyende pakati pa masautso, mumasunga moyo wanga; mumatambasula dzanja lanu kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga, mumandipulumutsa ndi dzanja lanu lamanja.
Uray no magnaak iti tengnga ti peggad, saluadamto ti biagko; igaw-atmonto ti imam iti unget dagiti kabusorko, ken ispalennakto ti makannawan nga imam.
8 Yehova adzakwaniritsa cholinga chake pa ine; chikondi chanu chosasinthika Yehova, ndi chosatha musasiye ntchito ya manja anu.
Kaduak ni Yahweh anggingga iti panungpalan; ti kinapudnom iti tulagmo, O Yahweh, ket agnanayon; saanmo a baybay-an dagiti inaramid dagiti imam.

< Masalimo 138 >