< Masalimo 138 >

1 Salimo la Davide. Ndidzakuyamikani Yehova ndi mtima wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zokutamandani pamaso pa “milungu.”
Par David. Je te rendrai grâce de tout mon cœur. Devant les dieux, je chanterai tes louanges.
2 Ndidzagwada kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera ndipo ndidzayamika dzina lanu chifukwa cha chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu, pakuti Inu mwakuza dzina lanu ndi mawu anu kupambana zinthu zonse.
Je me prosternerai devant ton temple saint, et rendre grâce à ton Nom pour ta bonté et ta vérité; car tu as exalté ton Nom et ta Parole au-dessus de tout.
3 Pamene ndinayitana, munandiyankha; munandisandutsa wamphamvu ndi wolimba mtima.
Le jour où j'ai appelé, tu m'as répondu. Vous m'avez encouragé avec la force dans mon âme.
4 Mafumu onse a dziko lapansi akuyamikeni Yehova, pamene amva mawu a pakamwa panu.
Tous les rois de la terre te rendront grâce, Yahvé, car ils ont entendu les paroles de ta bouche.
5 Iwo ayimbe za njira za Yehova, pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukulu.
Oui, ils chanteront les voies de Yahvé, car la gloire de Yahvé est grande!
6 Ngakhale kuti Yehova ngokwezeka, amasamalira odzichepetsa, koma anthu onyada amawadziwira chapatali.
Car si Yahvé est élevé, il prend soin des humbles; mais il connaît l'orgueilleux de loin.
7 Ngakhale ndiyende pakati pa masautso, mumasunga moyo wanga; mumatambasula dzanja lanu kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga, mumandipulumutsa ndi dzanja lanu lamanja.
Quand je marche au milieu de la détresse, tu me fais revivre. Tu étendras ta main contre la colère de mes ennemis. Ta main droite me sauvera.
8 Yehova adzakwaniritsa cholinga chake pa ine; chikondi chanu chosasinthika Yehova, ndi chosatha musasiye ntchito ya manja anu.
L'Éternel accomplira ce qui me concerne. Ta bonté, Yahvé, dure à jamais. N'abandonnez pas le travail de vos propres mains.

< Masalimo 138 >