< Masalimo 138 >
1 Salimo la Davide. Ndidzakuyamikani Yehova ndi mtima wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zokutamandani pamaso pa “milungu.”
`To Dauith him silf. Lord, Y schal knouleche to thee in al myn herte; for thou herdist the wordis of my mouth. Mi God, Y schal singe to thee in the siyt of aungels;
2 Ndidzagwada kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera ndipo ndidzayamika dzina lanu chifukwa cha chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu, pakuti Inu mwakuza dzina lanu ndi mawu anu kupambana zinthu zonse.
Y schal worschipe to thin hooli temple, and Y schal knouleche to thi name. On thi merci and thi treuthe; for thou hast magnefied thin hooli name aboue al thing.
3 Pamene ndinayitana, munandiyankha; munandisandutsa wamphamvu ndi wolimba mtima.
In what euere dai Y schal inwardli clepe thee, here thou me; thou schalt multipli vertu in my soule.
4 Mafumu onse a dziko lapansi akuyamikeni Yehova, pamene amva mawu a pakamwa panu.
Lord, alle the kingis of erthe knouleche to thee; for thei herden alle the wordis of thi mouth.
5 Iwo ayimbe za njira za Yehova, pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukulu.
And singe thei in the weies of the Lord; for the glorie of the Lord is greet.
6 Ngakhale kuti Yehova ngokwezeka, amasamalira odzichepetsa, koma anthu onyada amawadziwira chapatali.
For the Lord is hiy, and biholdith meke thingis; and knowith afer hiy thingis.
7 Ngakhale ndiyende pakati pa masautso, mumasunga moyo wanga; mumatambasula dzanja lanu kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga, mumandipulumutsa ndi dzanja lanu lamanja.
If Y schal go in the myddil of tribulacioun, thou schalt quikene me; and thou stretchidist forth thin hond on the ire of myn enemyes, and thi riyt hond made me saaf.
8 Yehova adzakwaniritsa cholinga chake pa ine; chikondi chanu chosasinthika Yehova, ndi chosatha musasiye ntchito ya manja anu.
The Lord schal yelde for me, Lord, thi merci is with outen ende; dispise thou not the werkis of thin hondis.