< Masalimo 138 >

1 Salimo la Davide. Ndidzakuyamikani Yehova ndi mtima wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zokutamandani pamaso pa “milungu.”
[A Psalm] of David. I will give thee thanks with my whole heart: before the gods will I sing praises unto thee.
2 Ndidzagwada kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera ndipo ndidzayamika dzina lanu chifukwa cha chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu, pakuti Inu mwakuza dzina lanu ndi mawu anu kupambana zinthu zonse.
I will worship toward thy holy temple, and give thanks unto thy name for thy lovingkindness and for thy truth: for thou hast magnified thy word above all thy name.
3 Pamene ndinayitana, munandiyankha; munandisandutsa wamphamvu ndi wolimba mtima.
In the day that I called thou answeredst me, thou didst encourage me with strength in my soul.
4 Mafumu onse a dziko lapansi akuyamikeni Yehova, pamene amva mawu a pakamwa panu.
All the kings of the earth shall give thee thanks, O LORD, for they have heard the words of thy mouth.
5 Iwo ayimbe za njira za Yehova, pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukulu.
Yea, they shall sing of the ways of the LORD; for great is the glory of the LORD.
6 Ngakhale kuti Yehova ngokwezeka, amasamalira odzichepetsa, koma anthu onyada amawadziwira chapatali.
For though the LORD be high, yet hath he respect unto the lowly: but the haughty he knoweth from afar.
7 Ngakhale ndiyende pakati pa masautso, mumasunga moyo wanga; mumatambasula dzanja lanu kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga, mumandipulumutsa ndi dzanja lanu lamanja.
Though I walk in the midst of trouble, thou wilt revive me; thou shalt stretch forth thine hand against the wrath of mine enemies, and thy right hand shall save me.
8 Yehova adzakwaniritsa cholinga chake pa ine; chikondi chanu chosasinthika Yehova, ndi chosatha musasiye ntchito ya manja anu.
The LORD will perfect that which concerneth me: thy mercy, O LORD, [endureth] for ever; forsake not the works of thine own hands.

< Masalimo 138 >