< Masalimo 138 >
1 Salimo la Davide. Ndidzakuyamikani Yehova ndi mtima wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zokutamandani pamaso pa “milungu.”
Of David. I will thank you, O Lord, with all my heart: in the sight of the gods I will sing your praise,
2 Ndidzagwada kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera ndipo ndidzayamika dzina lanu chifukwa cha chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu, pakuti Inu mwakuza dzina lanu ndi mawu anu kupambana zinthu zonse.
and prostrate before your holy temple, will praise your name for your constant love, for you have exulted your promise above all.
3 Pamene ndinayitana, munandiyankha; munandisandutsa wamphamvu ndi wolimba mtima.
When I called you, you answered; you gave me strength, you inspired me.
4 Mafumu onse a dziko lapansi akuyamikeni Yehova, pamene amva mawu a pakamwa panu.
All the kings of the earth shall praise you, O Lord, when they shall have heard the words you have uttered;
5 Iwo ayimbe za njira za Yehova, pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukulu.
and they shall sing of the ways of the Lord, and tell of the Lord’s transcendent glory.
6 Ngakhale kuti Yehova ngokwezeka, amasamalira odzichepetsa, koma anthu onyada amawadziwira chapatali.
For, high though the Lord is, he looks on the lowly, and strikes down the haughty from far away.
7 Ngakhale ndiyende pakati pa masautso, mumasunga moyo wanga; mumatambasula dzanja lanu kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga, mumandipulumutsa ndi dzanja lanu lamanja.
Though my way be distressful, yet you preserve me: you lay your hand on my angry foes, and your right hand gives me victory.
8 Yehova adzakwaniritsa cholinga chake pa ine; chikondi chanu chosasinthika Yehova, ndi chosatha musasiye ntchito ya manja anu.
The Lord will accomplish all that which concerns me. Your kindness, O Lord, endures forever. O do not abandon the work of your hands.