< Masalimo 138 >
1 Salimo la Davide. Ndidzakuyamikani Yehova ndi mtima wanga wonse; ndidzayimba nyimbo zokutamandani pamaso pa “milungu.”
I will praise you with my whole heart: before the gods will I sing praise unto you.
2 Ndidzagwada kuyangʼana ku Nyumba yanu yoyera ndipo ndidzayamika dzina lanu chifukwa cha chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu, pakuti Inu mwakuza dzina lanu ndi mawu anu kupambana zinthu zonse.
I will worship toward your holy temple, and praise your name for your loving kindness and for your truth: for you have magnified your word above all your name.
3 Pamene ndinayitana, munandiyankha; munandisandutsa wamphamvu ndi wolimba mtima.
In the day when I cried you answered me, and strengthened me with strength in my soul.
4 Mafumu onse a dziko lapansi akuyamikeni Yehova, pamene amva mawu a pakamwa panu.
All the kings of the earth shall praise you, O LORD, when they hear the words of your mouth.
5 Iwo ayimbe za njira za Yehova, pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukulu.
Yea, they shall sing in the ways of the LORD: for great is the glory of the LORD.
6 Ngakhale kuti Yehova ngokwezeka, amasamalira odzichepetsa, koma anthu onyada amawadziwira chapatali.
Though the LORD be high, yet has he respect unto the lowly: but the proud he knows far off.
7 Ngakhale ndiyende pakati pa masautso, mumasunga moyo wanga; mumatambasula dzanja lanu kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga, mumandipulumutsa ndi dzanja lanu lamanja.
Though I walk in the midst of trouble, you will revive me: you shall stretch forth your hand against the wrath of mine enemies, and your right hand shall save me.
8 Yehova adzakwaniritsa cholinga chake pa ine; chikondi chanu chosasinthika Yehova, ndi chosatha musasiye ntchito ya manja anu.
The LORD will perfect that which concerns me: your mercy, O LORD, endures for ever: forsake not the works of your own hands.