< Masalimo 137 >

1 Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira pamene tinakumbukira Ziyoni.
На водама вавилонским сеђасмо и плакасмо опомињући се Сиона.
2 Kumeneko, pa mitengo ya misondozi tinapachika apangwe athu,
О врбама сред њега вешасмо харфе своје.
3 pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo. Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo; iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”
Онде искаху који нас заробише да певамо, и који нас оборише да се веселимо: "Певајте нам песму сионску."
4 Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova mʼdziko lachilendo?
Како ћемо певати песму Господњу у земљи туђој?
5 Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu, dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.
Ако заборавим тебе, Јерусалиме, нека ме заборави десница моја.
6 Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu, ngati sindiyesa iwe chimwemwe changa chachikulu.
Нека прионе језик мој за уста моја, ако тебе не успамтим, ако не уздржим Јерусалима сврх весеља свог.
7 Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita pa tsiku limene Yerusalemu anagonja. Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi mpaka pa maziko ake!”
Напомени, Господе, синовима Едомовим дан јерусалимски, кад говорише: Раскопајте, раскопајте га до темеља.
8 Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa, wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera pa zimene watichitira.
Кћери вавилонска, крвницо, благо ономе ко ти плати за дело које си нама учинила!
9 Amene adzagwira makanda ako ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.
Благо ономе који узме и разбије децу твоју о камен.

< Masalimo 137 >