< Masalimo 137 >

1 Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira pamene tinakumbukira Ziyoni.
Psalmus David, propter Hieremiam. Super flumina Babylonis, illic sedimus et flevimus: cum recordaremur Sion:
2 Kumeneko, pa mitengo ya misondozi tinapachika apangwe athu,
In salicibus in medio eius, suspendimus organa nostra.
3 pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo. Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo; iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”
Quia illic interrogaverunt nos, qui captivos duxerunt nos, verba cantionum: Et qui abduxerunt nos: Hymnum cantate nobis de canticis Sion.
4 Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova mʼdziko lachilendo?
Quomodo cantabimus canticum Domini in terra aliena?
5 Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu, dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.
Si oblitus fuero tui Ierusalem, oblivioni detur dextera mea.
6 Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu, ngati sindiyesa iwe chimwemwe changa chachikulu.
Adhaereat lingua mea faucibus meis, si non meminero tui: Si non proposuero Ierusalem, in principio laetitiae meae.
7 Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita pa tsiku limene Yerusalemu anagonja. Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi mpaka pa maziko ake!”
Memor esto Domine filiorum Edom, in die Ierusalem: Qui dicunt: Exinanite, exinanite usque ad fundamentum in ea.
8 Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa, wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera pa zimene watichitira.
Filia Babylonis misera: beatus, qui retribuet tibi retributionem tuam, quam retribuisti nobis.
9 Amene adzagwira makanda ako ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.
Beatus, qui tenebit, et allidet parvulos suos ad petram.

< Masalimo 137 >