< Masalimo 137 >

1 Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira pamene tinakumbukira Ziyoni.
Sui fiumi di Babilonia, là sedevamo piangendo al ricordo di Sion.
2 Kumeneko, pa mitengo ya misondozi tinapachika apangwe athu,
Ai salici di quella terra appendemmo le nostre cetre.
3 pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo. Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo; iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”
Là ci chiedevano parole di canto coloro che ci avevano deportato, canzoni di gioia, i nostri oppressori: «Cantateci i canti di Sion!».
4 Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova mʼdziko lachilendo?
Come cantare i canti del Signore in terra straniera?
5 Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu, dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.
Se ti dimentico, Gerusalemme, si paralizzi la mia destra;
6 Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu, ngati sindiyesa iwe chimwemwe changa chachikulu.
mi si attacchi la lingua al palato, se lascio cadere il tuo ricordo, se non metto Gerusalemme al di sopra di ogni mia gioia.
7 Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita pa tsiku limene Yerusalemu anagonja. Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi mpaka pa maziko ake!”
Ricordati, Signore, dei figli di Edom, che nel giorno di Gerusalemme, dicevano: «Distruggete, distruggete anche le sue fondamenta».
8 Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa, wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera pa zimene watichitira.
Figlia di Babilonia devastatrice, beato chi ti renderà quanto ci hai fatto.
9 Amene adzagwira makanda ako ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.
Beato chi afferrerà i tuoi piccoli e li sbatterà contro la pietra.

< Masalimo 137 >