< Masalimo 137 >

1 Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira pamene tinakumbukira Ziyoni.
על נהרות בבל שם ישבנו גם בכינו בזכרנו את ציון׃
2 Kumeneko, pa mitengo ya misondozi tinapachika apangwe athu,
על ערבים בתוכה תלינו כנרותינו׃
3 pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo. Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo; iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”
כי שם שאלונו שובינו דברי שיר ותוללינו שמחה שירו לנו משיר ציון׃
4 Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova mʼdziko lachilendo?
איך נשיר את שיר יהוה על אדמת נכר׃
5 Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu, dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.
אם אשכחך ירושלם תשכח ימיני׃
6 Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu, ngati sindiyesa iwe chimwemwe changa chachikulu.
תדבק לשוני לחכי אם לא אזכרכי אם לא אעלה את ירושלם על ראש שמחתי׃
7 Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita pa tsiku limene Yerusalemu anagonja. Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi mpaka pa maziko ake!”
זכר יהוה לבני אדום את יום ירושלם האמרים ערו ערו עד היסוד בה׃
8 Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa, wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera pa zimene watichitira.
בת בבל השדודה אשרי שישלם לך את גמולך שגמלת לנו׃
9 Amene adzagwira makanda ako ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.
אשרי שיאחז ונפץ את עלליך אל הסלע׃

< Masalimo 137 >