< Masalimo 137 >

1 Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira pamene tinakumbukira Ziyoni.
By the rivers of Babylon, there we sat down. Yes, we wept, when we remembered Zion.
2 Kumeneko, pa mitengo ya misondozi tinapachika apangwe athu,
On the willows in that land, we hung up our harps.
3 pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo. Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo; iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”
For there, those who led us captive asked us for songs. Those who tormented us demanded songs of joy: “Sing us one of the songs of Zion!”
4 Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova mʼdziko lachilendo?
How can we sing Yahweh’s song in a foreign land?
5 Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu, dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.
If I forget you, Jerusalem, let my right hand forget its skill.
6 Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu, ngati sindiyesa iwe chimwemwe changa chachikulu.
Let my tongue stick to the roof of my mouth if I don’t remember you, if I don’t prefer Jerusalem above my chief joy.
7 Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita pa tsiku limene Yerusalemu anagonja. Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi mpaka pa maziko ake!”
Remember, Yahweh, against the children of Edom in the day of Jerusalem, who said, “Raze it! Raze it even to its foundation!”
8 Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa, wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera pa zimene watichitira.
Daughter of Babylon, doomed to destruction, he will be happy who repays you, as you have done to us.
9 Amene adzagwira makanda ako ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.
Happy shall he be, who takes and dashes your little ones against the rock.

< Masalimo 137 >