< Masalimo 137 >

1 Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira pamene tinakumbukira Ziyoni.
By the rivers of Babylon, there, we sat down, yea we wept—when we remembered Zion:
2 Kumeneko, pa mitengo ya misondozi tinapachika apangwe athu,
Upon the willows—in the midst thereof, hanged we our lyres:
3 pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo. Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo; iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”
For, there, our captors asked of us words of song, and our plunderers—gladness, —Sing us of the songs of Zion!
4 Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova mʼdziko lachilendo?
How shall we sing the song of Yahweh, on a foreign soil?
5 Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu, dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.
If I forget thee, O Jerusalem, Let my right-hand forget:
6 Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu, ngati sindiyesa iwe chimwemwe changa chachikulu.
Let my tongue cleave to the roof of my mouth, if I do not remember thee! if I do not lift up Jerusalem above the head of mine own gladness.
7 Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita pa tsiku limene Yerusalemu anagonja. Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi mpaka pa maziko ake!”
Remember, O Yahweh, against the sons of Edom, the day of Jerusalem, —how they continued to say—Overthrow! Overthrow! unto the foundation within it.
8 Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa, wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera pa zimene watichitira.
O ruined daughter of Babylon, —how happy the man who shall repay thee thy dealing, wherewith thou didst deal with us!
9 Amene adzagwira makanda ako ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.
How happy the man who shall snatch away and dash thy children against the crag.

< Masalimo 137 >