< Masalimo 137 >

1 Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira pamene tinakumbukira Ziyoni.
By the riuers of Babel we sate, and there wee wept, when we remembred Zion.
2 Kumeneko, pa mitengo ya misondozi tinapachika apangwe athu,
Wee hanged our harpes vpon the willowes in the middes thereof.
3 pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo. Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo; iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”
Then they that ledde vs captiues, required of vs songs and mirth, when wee had hanged vp our harpes, saying, Sing vs one of the songs of Zion.
4 Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova mʼdziko lachilendo?
Howe shall we sing, said we, a song of the Lord in a strange land?
5 Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu, dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.
If I forget thee, O Ierusalem, let my right hand forget to play.
6 Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu, ngati sindiyesa iwe chimwemwe changa chachikulu.
If I do not remember thee, let my tongue cleaue to the roofe of my mouth: yea, if I preferre not Ierusalem to my chiefe ioy.
7 Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita pa tsiku limene Yerusalemu anagonja. Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi mpaka pa maziko ake!”
Remember the children of Edom, O Lord, in the day of Ierusalem, which saide, Rase it, rase it to the foundation thereof.
8 Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa, wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera pa zimene watichitira.
O daughter of Babel, worthy to be destroyed, blessed shall he be that rewardeth thee, as thou hast serued vs.
9 Amene adzagwira makanda ako ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.
Blessed shall he be that taketh and dasheth thy children against the stones.

< Masalimo 137 >