< Masalimo 137 >

1 Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira pamene tinakumbukira Ziyoni.
Na obali rijeka babilonskih sjeđasmo i plakasmo spominjući se Siona;
2 Kumeneko, pa mitengo ya misondozi tinapachika apangwe athu,
o vrbe naokolo harfe svoje bijasmo povješali.
3 pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo. Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo; iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”
I tada naši tamničari zaiskaše od nas da pjevamo, porobljivači naši zaiskaše da se veselimo: “Pjevajte nam pjesmu sionsku!”
4 Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova mʼdziko lachilendo?
Kako da pjesmu Jahvinu pjevamo u zemlji tuđinskoj!
5 Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu, dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.
Nek' se osuši desnica moja, Jeruzaleme, ako tebe zaboravim!
6 Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu, ngati sindiyesa iwe chimwemwe changa chachikulu.
Nek' mi se jezik za nepce prilijepi ako spomen tvoj smetnem ja ikada, ako ne stavim Jeruzalem vrh svake radosti svoje!
7 Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita pa tsiku limene Yerusalemu anagonja. Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi mpaka pa maziko ake!”
Ne zaboravi, Jahve, sinovima Edoma kako su u dan kobni Jeruzalemov vikali oni: “Rušite! Srušite ga do temelja!”
8 Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa, wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera pa zimene watichitira.
Kćeri babilonska, pustošiteljice, blažen koji ti vrati milo za drago za sva zla što si nam ih nanijela!
9 Amene adzagwira makanda ako ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.
Blažen koji zgrabi i smrska o stijenu tvoju dojenčad!

< Masalimo 137 >