< Masalimo 135 >

1 Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
Monkamfo Awurade. Monkamfo Awurade din; monkamfo no, mo Awurade asomfo,
2 amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
mo a mosom wɔ Awurade fi, wɔ adiwo a ɛwɔ yɛn Nyankopɔn fi.
3 Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
Monkamfo Awurade efisɛ oye; monto ayeyi nnwom mma ne din, na ɛno na ɛyɛ anisɔ.
4 Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
Awurade ayi Yakob sɛ ɔnyɛ ne de, wayi Israel sɛ nʼade a ɛsom bo.
5 Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
Minim sɛ Awurade so; Ɔso sen anyame nyinaa.
6 Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
Awurade yɛ nea ɔpɛ biara wɔ ɔsoro ne asase so, po ne mu bun nyinaa.
7 Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
Ɔma omununkum ma ne ho so fi asase ano ba; ɔsoma anyinam ka osu ho na ɔma ahum tu fi ne koradan mu.
8 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
Okum Misraim mmakan, nnipa ne mmoa mmakan.
9 Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
Ɔsomaa ne nsɛnkyerɛnne ne nʼanwonwade baa mo mfimfini, Misraim, de tiaa Farao ne nʼasomfo nyinaa.
10 Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
Ɔsɛee amanaman pii, na okunkum ahemfo akɛse,
11 Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
Amorifo hene, Sihon Basan hene, Og ne Kanaan ahemfo nyinaa,
12 ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
na ɔde wɔn nsase maa sɛ agyapade ɔde maa ne nkurɔfo Israelfo.
13 Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
Awurade, wo din wɔ hɔ daa. Awurade wo din ahyeta awo ntoatoaso nyinaa mu.
14 Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
Awurade bedi ama ne nkurɔfo na obehu nʼasomfo mmɔbɔ.
15 Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
Amanaman no ahoni yɛ dwetɛ ne sikakɔkɔɔ a wɔde onipa nsa na ayɛ.
16 Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
Wɔwɔ ano, nanso wontumi nkasa, wɔwɔ ani, nanso wonhu ade;
17 makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
wɔwɔ aso, nanso wɔnte asɛm, na ɔhome nso nni wɔn anom.
18 Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
Wɔn a wɔyɛɛ ahoni no bɛyɛ sɛ wɔn ara, saa ara na wɔn a wɔde wɔn ho to wɔn so no bɛyɛ.
19 Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
Monkamfo Awurade, mo Israelfo nyinaa; monkamfo Awurade, Aaron fi;
20 Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
monkamfo Awurade, Lewi fi; monkamfo Awurade, mo a musuro no.
21 Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.
Mumfi Sion nkamfo Awurade, monkamfo nea ɔte Yerusalem no. Monkamfo Awurade.

< Masalimo 135 >