< Masalimo 135 >

1 Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
Halleluja! Loven HERRENS namn, loven det, i HERRENS tjänare,
2 amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
I som stån i HERRENS hus, i gårdarna till vår Guds hus.
3 Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
Loven HERREN, ty HERREN är god, lovsjungen hans namn, ty det är ljuvligt.
4 Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
Se, HERREN har utvalt Jakob åt sig, Israel till sin egendom.
5 Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
Ty jag vet att HERREN är stor, att vår Herre är förmer än alla gudar.
6 Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
HERREN kan göra allt vad han vill, i himmelen och på jorden, i haven och i alla djup;
7 Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
han som låter regnskyar stiga upp från jordens ända, han som låter ljungeldar komma med regn och för vinden ut ur dess förvaringsrum;
8 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
han som slog de förstfödda i Egypten, både människor och boskap;
9 Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
han som sände tecken och under över dig, Egypten, över Farao och alla hans tjänare;
10 Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
han som slog stora folk och dräpte mäktiga konungar:
11 Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
Sihon, amoréernas konung, och Og, konungen i Basan, med alla Kanaans riken,
12 ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
och gav deras land till arvedel, till arvedel åt sitt folk Israel.
13 Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
HERRE, ditt namn varar evinnerligen, HERRE, din åminnelse från släkte till släkte.
14 Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
Ty HERREN skaffar rätt åt sitt folk, och över sina tjänare förbarmar han sig.
15 Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
Hedningarnas avgudar äro silver och guld, verk av människohänder.
16 Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
De hava mun och tala icke, de hava ögon och se icke,
17 makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
de hava öron och lyssna icke till, och ingen ande är i deras mun.
18 Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
De som hava gjort dem skola bliva dem lika, ja, alla som förtrösta på dem.
19 Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
I av Israels hus, loven HERREN; I av Arons hus, loven HERREN;
20 Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
I av Levis hus, loven HERREN; I som frukten HERREN, loven HERREN.
21 Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.
Lovad vare HERREN från Sion, han som bor i Jerusalem! Halleluja! Se Frukta Gud i Ordförkl.

< Masalimo 135 >