< Masalimo 135 >
1 Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
Aleluia! Louvai o nome do SENHOR; louvai [-o] vós, servos do SENHOR,
2 amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
Que prestais serviço na Casa do SENHOR, nos pátios da Casa do nosso Deus.
3 Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
Louvai ao SENHOR, porque o SENHOR é bom; cantai louvores ao seu nome, porque é agradável;
4 Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
Porque o SENHOR escolheu para si a Jacó, a Israel como propriedade sua;
5 Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
Porque eu sei que o SENHOR é grande, e nosso Senhor está acima de todos os deuses.
6 Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
O SENHOR faz tudo o que quer, nos céus, na terra, nos mares, e [em] todos os abismos.
7 Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
Ele faz as nuvens subirem desde os confins da terra, faz os relâmpagos com a chuva; ele produz os ventos de seus tesouros.
8 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
Ele feriu os primogênitos do Egito, desde os homens até os animais.
9 Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
Ele enviou sinais e prodígios no meio de ti, Egito; contra Faraó, e contra todos os seus servos.
10 Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
Ele feriu muitas nações, e matou reis poderosos:
11 Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
Seom, rei dos amorreus, e Ogue, rei de Basã; e todos os reinos de Canaã.
12 ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
E deu a terra deles como herança; como herança a Israel, seu povo.
13 Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
Ó SENHOR, teu nome [dura] para sempre; [e] tua memória, SENHOR, de geração em geração.
14 Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
Porque o SENHOR julgará a seu povo; e terá compaixão de seus servos.
15 Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
Os ídolos das nações [são] prata e ouro; [são] obra de mãos humanas.
16 Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
Têm boca, mas não falam; têm olhos, mas não veem.
17 makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
Têm ouvidos, mas não ouvem; não têm respiração em sua boca.
18 Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
Tornem-se como eles os que os fazem, [e] todos os que confiam neles.
19 Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
Casa de Israel, bendizei ao SENHOR! Casa de Arão, bendizei ao SENHOR!
20 Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
Casa de Levi, bendizei ao SENHOR! Vós que temeis ao SENHOR, bendizei ao SENHOR.
21 Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.
Bendito seja o SENHOR desde Sião, ele que habita em Jerusalém. Aleluia!