< Masalimo 135 >
1 Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
Halleluja. Chwalcie imię Pańskie, chwalcie słudzy Pańscy.
2 amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
Którzy stawacie w domu Pańskim, w sieniach domu Boga naszego.
3 Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
Chwalcież Pana, albowiem to Pan dobry; śpiewajcież imieniowi jego, boć jest wdzięczne.
4 Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
Albowiem sobie Jakóba Pan obrał, i Izraela za własność swoję.
5 Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
Jać zaiste uznaję, iż wielki jest Pan, a Pan nasz jest nad wszystkich bogów.
6 Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
Wszystko co chce Pan, to czyni, na niebie i na ziemi, w morzu i we wszystkich przepaściach.
7 Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
Który czyni, że występują pary od kończyn ziemi; błyskawice i dżdże przywodzi, wywodzi wiatr z skarbów swoich;
8 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
Który pobił pierworodztwa w Egipcie, od człowieka aż do bydlęcia.
9 Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
Posłał znaki i cuda w pośród ciebie, Egipcie! na Faraona i na wszystkich sług jego.
10 Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
Który poraził wiele narodów, a pobił królów możnych;
11 Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
Sehona, króla Amorejskiego, i Oga, króla Basańskiego, i wszystkie królestwa Chananejskie.
12 ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
I dał ziemię ich w dziedzictwo, w dziedzictwo Izraelowi, ludowi swemu.
13 Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
Panie! imię twoje na wieki; Panie! pamiątka twoja od narodu do narodu.
14 Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
Zaite Pan sądzić będzie lud swój, a nad sługami swymi zmiłuje się.
15 Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
Ale bałwany pogańskie, srebro i złoto, są robotą rąk ludzkich.
16 Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
Usta mają, a nie mówią, oczy mają, a nie widzą;
17 makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
Uszy mają, a nie słyszą, ani mają tchnienia w ustach swoich.
18 Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
Niech im podobni będą, którzy je robią, i wszyscy, którzy w nich ufają.
19 Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
Domie Izraelski! błogosławcie Panu; domie Aaronowy! błogosławcie Panu.
20 Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
Domie Lewiego! błogosławcie Panu, którzy się boicie Pana, błogosławcie Panu.
21 Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.
Błogosławiony Pan z Syonu, który mieszka w Jeruzalemie. Halleluja.