< Masalimo 135 >
1 Tamandani Yehova. Tamandani dzina la Yehova; mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
Louez l'Éternel! Louez le nom de l'Éternel; louez-le, serviteurs de l'Éternel!
2 amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova, mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
Vous qui vous tenez dans la maison de l'Éternel, dans les parvis de la maison de notre Dieu,
3 Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino; imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
Louez l'Éternel, car l'Éternel est bon! Chantez à son nom, car il est clément!
4 Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake, Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.
Car l'Éternel s'est choisi Jacob et Israël pour sa possession.
5 Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu, kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
Car je sais que l'Éternel est grand, et notre Seigneur au-dessus de tous les dieux.
6 Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera, kumwamba ndi dziko lapansi, ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
L'Éternel fait tout ce qui lui plaît dans les cieux et sur la terre, dans les mers et dans tous les abîmes.
7 Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.
C'est lui qui fait monter du bout de la terre les vapeurs; qui produit les éclairs et la pluie; qui tire le vent de ses trésors.
8 Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
C'est lui qui a frappé les premiers-nés d'Égypte, depuis les hommes jusqu'aux bêtes;
9 Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto, kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
Qui a envoyé des signes et des prodiges au milieu de toi, Égypte, contre Pharaon et contre tous ses serviteurs;
10 Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu ndi kupha mafumu amphamvu:
Qui a frappé plusieurs nations, et mis à mort de puissants rois:
11 Sihoni mfumu ya Aamori, Ogi mfumu ya Basani, ndi maufumu onse a ku Kanaani;
Sihon, roi des Amoréens, et Og, roi de Bassan, et tous les rois de Canaan;
12 ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa, cholowa cha anthu ake Aisraeli.
Et qui a donné leur pays en héritage, en héritage à Israël, son peuple.
13 Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya, mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
Éternel, ton nom subsiste à toujours; Éternel, ta mémoire est d'âge en âge.
14 Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa, ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.
Car l'Éternel fera justice à son peuple, et il aura compassion de ses serviteurs.
15 Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
Les idoles des nations sont de l'argent et de l'or, un ouvrage de mains d'homme.
16 Pakamwa ali napo koma sayankhula maso ali nawo, koma sapenya;
Elles ont une bouche, et ne parlent point; elles ont des yeux, et ne voient point;
17 makutu ali nawo, koma sakumva ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
Elles ont des oreilles, et n'entendent point; il n'y a pas non plus de souffle dans leur bouche.
18 Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo, chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.
Ceux qui les font et tous ceux qui s'y confient leur deviendront semblables!
19 Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova; inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
Maison d'Israël, bénissez l'Éternel! Maison d'Aaron, bénissez l'Éternel!
20 Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova; Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
Maison de Lévi, bénissez l'Éternel! Vous qui craignez l'Éternel, bénissez l'Éternel!
21 Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni, amene amakhala mu Yerusalemu. Tamandani Yehova.
Béni soit, de Sion, l'Éternel qui réside à Jérusalem! Louez l'Éternel!